-
Mfundo Zazikulu za M’mabuku a Yoweli ndi AmosiNsanja ya Olonda—2007 | October 1
-
-
2:32—Kodi ‘kuitana pa dzina la Yehova’ kumatanthauza chiyani? Kuitana pa dzina la Mulungu kumatanthauza kudziwa bwino dzinali, kulilemekeza kwambiri, ndiponso kudalira ndi kukhulupirira mwini wake wa dzinalo.—Aroma 10:13, 14.
-
-
Mfundo Zazikulu za M’mabuku a Yoweli ndi AmosiNsanja ya Olonda—2007 | October 1
-
-
2:28-32. Anthu okhawo amene “adzaitana pa dzina la Yehova adzapulumutsidwa” pa “tsiku la Yehova lalikulu ndi loopsa.” Ndife oyamikira kuti Yehova amatsanulira mzimu wake pa anthu onse ndipo walola kuti ana ndi akulu omwe, amuna ndi akazi, agwire nawo ntchito yonenera, kapena kuti kulengeza “zinthu zazikulu za Mulungu.” (Machitidwe 2:11) Popeza tsiku la Yehova layandikira, tiyenera kukulitsa “khalidwe loyera” ndiponso kuchita ‘ntchito za kudzipereka kwa Mulungu.’—2 Petulo 3:10-12.
-