-
Machenjezo Aumulungu Amene AmakuyambukiraniNsanja ya Olonda—1989 | April 15
-
-
Palibe aliyense amene angapulumuke chiweruzo cha Yehova. Ulosi wa Obadiya, woperekedwa chifupifupi 607 B.C.E., unaneneratu za kuthamangitsidwa kwa Aedomu kuchoka m’dziko lawo mosasamala kanthu za malo awo owoneka kukhala achisungiko okwezeka “pakati pa nyenyezi.” Ndipo ngakhale kuti moyo waumunthu wa wolemba Baibulo ameneyu sunavumbulidwe, iye akukhalira moyo ku tanthauzo la dzina lake, “Mtumiki wa Yehova.” Motani? Mwa kulengeza chiweruzo chosakaza. Pamene Edomu akugwa, iye adzalandidwa kotheratu ndi mabwenzi amene ali m’pangano ndi iye. Osati ngakhale anzeru kapena amphamvu ake akapulumuka.—1-9.
-
-
Machenjezo Aumulungu Amene AmakuyambukiraniNsanja ya Olonda—1989 | April 15
-
-
○ 7—Mu nthaŵi za Baibulo, “kudya chakudya” pamodzi ndi munthu wina kunali kwenikweni pangano la unansi. Nchopyoza chotani nanga! Ababulo, “akupangana nawo” ndi Aedomu, akatsimikizira kukhala owawononga. Mowonadi, Ababulo a tsiku la Nebukadinezara analola Edomu kutengamo mbali m’kufunkha Yuda pambuyo pa kukhalitsidwa bwinja kwa Yerusalemu. Koma mfumu ya Babulo ya pambuyo pake Nabonidus kamodzi ndipo kwa nthaŵi zonse inathetsa zikhumbo za Edomu za chuma ndi malonda.
-