-
Muzikhulupirira Yehova Kuti Mukhale ndi MoyoNsanja ya Olonda (Yophunzira)—2018 | November
-
-
15, 16. (a) Kodi m’buku la Habakuku muli malonjezo otani? (b) Kodi tikuphunzira chiyani pa malonjezo amenewa?
15 Yehova analonjeza anthu olungama amene amamukhulupirira kuti: “Wolungama adzakhalabe ndi moyo mwa chikhulupiriro chake. Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi anthu odziwa ulemerero wa Yehova ngati mmene madzi amadzazira nyanja.” (Hab. 2:4, 14) Malinga ndi lembali, anthu amene amakhulupirira Yehova n’kumamuyembekezera moleza mtima adzalandira moyo wosatha.
-
-
Muzikhulupirira Yehova Kuti Mukhale ndi MoyoNsanja ya Olonda (Yophunzira)—2018 | November
-
-
17. Kodi Yehova watitsimikizira mfundo ziti m’buku la Habakuku?
17 M’buku la Habakuku muli phunziro lofunika kwambiri kwa anthu amene tikukhala m’masiku otsirizafe. Yehova akutitsimikizira kuti adzapereka moyo wosatha kwa wolungama aliyense amene amasonyeza kuti amamukhulupirira. Choncho kaya tikumane ndi mavuto otani, tiyeni tizilimbitsa chikhulupiriro chathu mwa Yehova. M’buku la Habakuku, Yehova watitsimikiziranso kuti adzatithandiza komanso kutipulumutsa. Iye amangotipempha kuti tizimukhulupirira komanso kuyembekezera moleza mtima Ufumu wake. Mu Ufumuwo, padziko lonse padzakhala atumiki ake ofatsa komanso osangalala okhaokha.—Mat. 5:5; Aheb. 10:36-39.
-