-
“Tipita Nanu Limodzi”Nsanja ya Olonda (Yophunzira)—2016 | January
-
-
1, 2. (a) Kodi Yehova ananeneratu kuti m’nthawi yathu ino kudzachitika zinthu zotani? (b) Kodi m’nkhaniyi tikambirana mafunso ati? (Onani chithunzi pamwambapa.)
PONENA za nthawi yathu ino, Yehova analosera kuti: “Amuna 10 ochokera m’zilankhulo zonse za anthu amitundu ina adzagwira chovala cha munthu amene ndi Myuda ndi kunena kuti: ‘Anthu inu tipita nanu limodzi, chifukwa tamva kuti Mulungu ali ndi inu.’” (Zek. 8:23) Mofanana ndi amuna 10 otchulidwa mulembali, anthu amene akuyembekezera kudzakhala padziko lapansi ‘agwira chovala cha munthu amene ndi Myuda.’ Iwo amasangalala kwambiri kuchita zinthu mogwirizana ndi “Isiraeli wa Mulungu,” kapena kuti odzozedwa, podziwa kuti Yehova akudalitsa anthuwa.—Agal. 6:16.
-
-
“Tipita Nanu Limodzi”Nsanja ya Olonda (Yophunzira)—2016 | January
-
-
4. Popeza n’zosatheka kudziwa mayina a odzozedwa onse amene ali padzikoli, kodi a nkhosa zina ‘angapite nawo’ bwanji?
4 Popeza panopa n’zosatheka kudziwa mayina a odzozedwa onse, kodi a nkhosa zina ‘angapite nawo limodzi’ bwanji? Ulosi wa Zekariya uja umanena kuti anthu 10 “adzagwira chovala cha munthu amene ndi Myuda ndi kunena kuti: ‘Anthu inu tipita nanu limodzi, chifukwa tamva kuti Mulungu ali ndi inu.’” Ngakhale kuti lembali latchula “Myuda,” limasonyeza kuti mawuwa sakuimira munthu mmodzi koma gulu la odzozedwa. A nkhosa zina akudziwa zimenezi ndipo amatumikira Yehova limodzi ndi gululi. Sikuti amafunika kudziwa munthu aliyense m’gululi n’kumamutsatira. Yesu ndiye Mtsogoleri wathu ndipo Baibulo limati tiyenera kutsatira iye yekha basi.—Mat. 23:10.
-