-
Ndinu Wofunika Kwambiri kwa Mulungu!Galamukani!—1999 | June 8
-
-
Mwachitsanzo, Yesu, pochitira fanizo kufunika kwa aliyense wa ophunzira ake, anati: “Kodi mpheta ziŵiri sizigulidwa kakhobiri? Ndipo imodzi ya izo siigwa pansi popanda Atate wanu [kudziŵa, NW]: komatu inu, matsitsi onse a m’mutu mwanu aŵerengedwa. Chifukwa chake musamawopa; inu mupambana mpheta zambiri.” (Mateyu 10:29-31) Taganizirani mmene mawu amenewo analimbikitsira omvetsera a Yesu a m’zaka za zana loyamba.
-
-
Ndinu Wofunika Kwambiri kwa Mulungu!Galamukani!—1999 | June 8
-
-
Kodi mukulimvetsetsa fanizo la Yesu lotonthoza mtimali? Ngati Yehova amaona kuti ngakhale timbalame ting’onoting’ono n’tofunika kwambiri kwa iye, nanga kuli bwanji ndi atumiki ake a padziko lapansi! Yehova amatizindikira ngakhale tili m’chigulu. Tonsefe Yehova amationa monga ofunika kwambiri kwa iye motero amayang’ana chilichonse cha ife—tsitsi lathu lenilenili, amaliŵerenga palokha palokha.
-