-
Kuyesetsa Kuti Anthu Mumpingo Apitirize Kukhala Amtendere Komanso OyeraGulu Lochita Chifuniro cha Mulungu
-
-
14 Yesu anafotokoza njira yothetsera mavuto obwera chifukwa choti Akhristu awiri asemphana maganizo pa nkhani zikuluzikulu. Taonani zinthu zitatu zimene ananena. Anati: “Ngati m’bale wako wachimwa, [1] upite kukam’fotokozera cholakwacho panokha iwe ndi iyeyo. Ngati wakumvera, ndiye kuti wabweza m’bale wakoyo. Koma akapanda kukumvera, [2] upiteko ndi munthu wina mmodzi kapena awiri, kuti nkhani yonse ikatsimikizike ndi pakamwa pa mboni ziwiri kapena zitatu. Akapanda kuwamvera amenewanso, [3] uuze mpingo. Ndipo akapandanso kumvera mpingowo, kwa iwe akhale ngati munthu wochokera mu mtundu wina komanso ngati wokhometsa msonkho.”—Mat. 18:15-17.
-
-
Kuyesetsa Kuti Anthu Mumpingo Apitirize Kukhala Amtendere Komanso OyeraGulu Lochita Chifuniro cha Mulungu
-
-
18 Ngati mwalephera kubweza mbale wanu mutamufotokozera cholakwacho ‘panokha inuyo ndi iyeyo,’ mungachite zimene Yesu ananena, zoti ‘mupiteko ndi munthu wina mmodzi kapena awiri’ n’kukakambirana nayenso. Amene mwawatengawo ayeneranso kukhala ndi cholinga chofuna kubweza mbale wanuyo. Zingakhale bwino ngati mutatenga anthu amene analipo pamene munthuyo ankapalamula mlanduwo. Koma ngati palibe anthu ena amene anaona zinthuzo zikuchitika, mungasankhe abale ena kuti akakhale mboni pamene mukukambirana nkhaniyo. Abalewo akhale oti akudziwa bwino mmene nkhani za mtundu umenewo zimayendera kuti athe kudziwa ngati zinthu zinalakwikadi kapena ayi. Akulu amene mungawasankhe kuti akhale mboni saimira mpingo, chifukwa sanachite kusankhidwa ndi bungwe la akulu.
-