Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mungabweze Mbale Wanu
    Nsanja ya Olonda—1999 | October 15
    • 5, 6. Malinga ndi nkhani yake, kodi Mateyu 18:15 anali kunena za machimo otani, ndipo n’chiyani chikusonyeza zimenezo?

      5 Malangizo a Yesu amakhudza makamaka nkhani zazikulu. Yesu anati: “Ngati mbale wako akuchimwira iwe.” M’lingaliro lalikulu, ‘tchimo’ lingakhale kulakwa kapena kuphophonya kwina kulikonse. (Yobu 2:10; Miyambo 21:4; Yakobo 4:17) Komabe, nkhani yake ikusonyeza kuti Yesu anali kutanthauza tchimo lalikulu. Linali lalikulu lomwe likanapangitsa wolakwayo kuonedwa “monga wakunja ndi wamsonkho.” Kodi mawu amenewo amatanthauzanji?

      6 Ophunzira a Yesu omwe anali kumvetsera mawu amenewo anali kudziŵa kuti ayuda anzawo sanali kuyenderana ndi Akunja. (Yohane 4:9; 18:28; Machitidwe 10:28) Ndipo anali kupeŵa amsonkho, anthu amene anali Ayuda koma amene anasanduka kukhala ochitira anzawo zoipa. Choncho nkhani ya pa Mateyu 18:15-17 inkanena za machimo aakulu, osati kusiyana maganizo kapena kukhumudwitsana kumene mutha kungokhululukira ndi kukuiŵala.​—Mateyu 18:21, 22.a

  • Mungabweze Mbale Wanu
    Nsanja ya Olonda—1999 | October 15
    • a Buku lotchedwa Cyclopedia lolembedwa ndi McClintock ndi Strong limati: “Amsonkho otchulidwa m’Chipangano Chatsopano ankaonedwa monga akapirikoni ndi am’patuko, odetsedwa chifukwa cha kuyanjana kwawo nthaŵi zonse ndi anthu akunja, pokhala ziŵiya za opondereza. Anali kuwaika m’gulu limodzi ndi ochimwa . . . Posankhulidwa chotero ndiponso kupeŵedwa ndi anthu a moyo wabwino, mabwenzi awo okha kapena anzawo anali kupezeka pakati pa awo amene anali anthu okanidwa ofanana ndi iwo.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena