-
Antchito m’Munda WampesaNsanja ya Olonda—1989 | August 15
-
-
Mwini banjayo, kapena mwini wa munda wampesayo, ali Yehova Mulungu, ndipo munda wampesawo uli mtundu wa Israyeli. Antchito m’munda wampesawo ali anthu omwe abweretsedwa mu pangano la Chilamulo; iwo mwachindunji ali Ayuda okhala m’masiku a atumwi. Chiri kokha ndi antchito a tsiku lonse omwe chivomerezo cha malipiro chapangidwa. Malipirowa ali rupiya latheka limodzi tsiku limodzi. Popeza kuti “dzuŵa litakwera” iri nthaŵi ya 9:00 a.m., awo oitanidwa dzuŵa litakwera, usana, popendeka dzuŵa, ndi madzulo akugwira ntchito, aliyense payekha, kokha maora 9, 6, 3, ndi 1.
Antchito a maora 12, kapena tsiku lonse, akuimira atsogoleri Achiyuda omwe akhala otanganitsidwa mopitirizabe mu utumiki wa chipembedzo. Iwo sali ofanana ndi ophunzira a Yesu, omwe, kwa mbali yaikulu ya miyoyo yawo, anakhala olembedwa ntchito m’kusodza kapena ntchito zina zakudziko. Osati kufikira mu chirimwe cha 29 C.E. ndipamene “mwini banja” anatumiza Yesu Kristu kudzasonkhanitsa amenewa kukhala ophunzira ake. Iwo mwakutero anakhala “akuthungo,” kapena antchito a madzulo m’munda wampesa.
-
-
Antchito m’Munda WampesaNsanja ya Olonda—1989 | August 15
-
-
Kulandiridwa kwa rupiya latheka kunachitika, osati pa imfa ya Yesu, koma pa Pentekoste wa 33 C.E., pamene Kristu, “kapitawo,” anatsanulira mzimu woyera pa ophunzira ake. Ophunzira a Yesu amenewa anali ofanana ndi “omalizira,” kapena antchito otuluka madzulo.
-
-
Antchito m’Munda WampesaNsanja ya Olonda—1989 | August 15
-
-
Kodi kukwaniritsidwa kwa m’zana loyamba kumeneku kuli kukwaniritsidwa kokha kwa fanizo la Yesu? Ayi, atsogoleri achipembedzo a Chikristu cha Dziko m’zana la 20 lino, chifukwa cha malo awo ndi mathayo, akhala “oyamba” kulembedwa ntchito m’munda wampesa wophiphiritsira wa Mulungu. Iwo analingalira olalikira odzipereka oyanjana ndi Watch Tower Bible and Tract Society kukhala “omalizira” kukhala ndi thayo lirilonse lotsimikizirika mu utumiki wa Mulungu. Koma, m’chenicheni, ali amenewa amene atsogoleri achipembedzo ananyoza omwe alandira rupiya latheka—ulemu wa kutumikira monga oimira odzozedwa a Ufumu wakumwamba wa Mulungu. Mateyu 19:30–20:16.
-