-
“Kodi Nchiyani Chidzakhala Chizindikiro cha Kukhalapo Kwanu”?Nsanja ya Olonda—1994 | February 15
-
-
“POMWEPO” Chimaliziro
10. Kodi nchifukwa ninji tiyenera kuzindikira liwu Lachigiriki lakuti toʹte, ndipo limatanthauzanji?
10 M’mbali zina Yesu anafotokoza zochitikazo kukhala zikuchitika motsatizana. Iye anati: “Uthenga uwu wabwino wa ufumu udzalalikidwa . . . ndipo pomwepo chidzafika chimaliziro.” Kaŵirikaŵiri Mabaibulo a m’Chingelezi amagwiritsira ntchito liwulo “pomwepo” ndi tanthauzo losavuta lakuti “chotero” kapena “koma.” (Marko 4:15, 17; 13:23) Komabe, pa Mateyu 24:14, “pomwepo” ndiliwu lozikidwa pa adiverebu Yachigiriki yakuti toʹte.c Akatswiri Achigiriki amanena kuti liwu lakuti toʹte ndilo “adiverebu yosonyeza nthaŵi” yogwiritsiridwa ntchito “kudziŵikitsa chimene chikutsatira nthaŵiyo” kapena “kudziŵikitsa chochikitika chotsatirapo.” Chotero Yesu analosera kuti pakakhala kulalikidwa kwa Ufumu ndipo pomwepo (‘pambuyo pake’ kapena ‘ndiyeno’) chidzafika “chimaliziro.” Chimaliziro chiti?
-
-
“Kodi Nchiyani Chidzakhala Chizindikiro cha Kukhalapo Kwanu”?Nsanja ya Olonda—1994 | February 15
-
-
c Toʹte akupezeka nthaŵi zoposa 80 m’Mateyu (nthaŵi 9 m’chaputala 24) ndi nthaŵi 15 m’buku la Luka. Marko anagwiritsira ntchito toʹte nthaŵi zisanu ndi imodzi zokha, koma nthaŵi zinayi za izo zinali za “chizindikiro.”
-