-
Kukhala Olinganizidwa Kaamba ka Kupulumuka Kuloŵa m’Zaka ChikwiNsanja ya Olonda—1989 | September 1
-
-
6. (a) Kodi kubadwa kwa Ufumu kunaitanira kaamba ka ntchito yotani yonenedweratu ndi Yesu? (b) Kodi kuchita ntchito imeneyi kunaitanira kaamba ka chiyani ku mbali ya anthu a Yehova, ndipo kodi ndi mtundu wotani wa kupita patsogolo umene iwo tsopano akuwunikira?
6 Kubadwa kwa Ufumu wa Yehova kupyolera mwa umene iye adzakweza ulamuliro wake wolondola pa chilengedwe chaponseponse—aha, pano panali chinachake chomwe chinafunikira kulengezedwa m’dziko lonse lapansi! Ndipo tsopano inali nthaŵi ya kukwaniritsidwa kwa mawu awa a Yesu onena za zitsimikiziro za “kukhalapo” kwake kosawoneka: “Mbiri yabwino imeneyi ya ufumu idzalalikidwa m’dziko lonse lapansi lokhalidwa ndi anthu kaamba ka umboni kwa mitundu yonse; ndipo pomwepo mapeto adzafika.” (Mateyu 24:3, 14, NW) Kulalikira kogwirizana, komvana pa mlingo wa mitundu yonse, m’dziko lonse lapansi ndithudi kukaitanira kaamba ka kulinganiza mbali yowoneka ndi maso ya gulu la Yehova la chilengedwe chaponseponse. Watch Tower Bible and Tract Society, monga momwe inaimiridwa ndi yemwe pa nthaŵiyo anali prezidenti wake, J. F. Rutherford, inayanja chimenechi. Chotero, kuyambira m’chaka cha pambuyo pa nkhondo cha 1919, kulinganiza kwa achilikizi okhulupirika a Sosaite monga mtundu wobwezeretsedwa kunapita patsogolo mogamulapo, ndi pemphero kaamba ka chitsogozo ndi dalitso la Wolinganiza Wamkulu, Yehova Mulungu. Poyang’anizana ndi Nkhondo ya Dziko ya II, mosasamala kanthu za chizunzo choipitsitsa chochitidwa ndi Magulu Ankhanza, gulu la Nazi la Hitler, ndi Kachitidwe ka Chikatolika, Mboni za Yehova dziko lonse lapansi zinawunikira kupita patsogolo kogwirizana ku dziko la mdani.
-
-
Kukhala Olinganizidwa Kaamba ka Kupulumuka Kuloŵa m’Zaka ChikwiNsanja ya Olonda—1989 | September 1
-
-
9. Kodi nchifukwa ninji nkhosa zikuitanidwa kuloŵa “ufumu wokonzedwera kwa [iwo],” ndipo kodi ndimotani mmene iwo aliri m’malo abwino kwambiri akuchita zabwino kwa abale a Mfumuyo?
9 Kodi nchifukwa ninji onga nkhosa amenewa akuitanidwa “kuloŵa mu ufumu wokonzedwera kwa [iwo] pa chikhazikiro chake cha dziko lapansi”? Mfumuyo ikuwawuza iwo kuti chiri chifukwa chakuti iwo anachita zabwino kwa “abale” ake, ndipo mwakutero anachita chimenecho kwa iye. Ndi mawu akuti “abale,” Mfumuyo ikutanthauza otsalira a abale ake auzimu omwe adakali pa dziko lapansi m’mapeto ano a dongosolo la zinthu. Pokhala gulu limodzi ndi abale amenewa a Mbusa ndi Mfumu, Yesu Kristu, iwo akakhala mu unansi wathithithi wothekera ndi otsalira oterowo ndipo mwakutero akakhala m’malo abwino koposa a kuchita zabwino kwa iwo. Ngakhale m’njira ya zinthu zakuthupi, iwo akathandiza abale a Yesu kulalikira uthenga wa Ufumu wokhazikitsidwa dziko lonse mapeto asanadze. M’chiyang’aniro cha ichi, nkhosa zikawona kukhala wa mtengo wapatali mwaŵi wawo wa kukhala olinganizidwa ndi otsalira monga gulu limodzi la Mbusa mmodzi.
-
-
Kukhala Olinganizidwa Kaamba ka Kupulumuka Kuloŵa m’Zaka ChikwiNsanja ya Olonda—1989 | September 1
-
-
11. Kodi ndimotani mmene nkhosa zimasonyezera kuti zimaima kaamba ka Ufumu, ndipo chifukwa cha ichi, kodi ndi dalitso lotani limene liri lawo?
11 Mosiyana ndi mbuzi zophiphiritsira, onga nkhosawo amasonyeza mosalakwika kuti akuchirikiza Ufumuwo. Motani? Mwa makhalidwe, osati kokha mawu. Chifukwa cha kusawoneka ndi maso kwa Mfumuyo m’mwamba, iwo sangachite zabwino mwachindunji kwa iye m’kuchirikiza Ufumu wake. Chotero iwo amachita zabwino kwa abale ake auzimu omwe adakali pa dziko lapansi. Ngakhale kuti ichi chimabweretsa udani, chitsutso, ndi chizunzo kumbali ya mbuzi, kaamba ka kuchita zabwino koteroko, nkhosazo zikuwuzidwa ndi Mfumuyo kuti izo ziri ‘zodalitsidwa ndi Atate wake.’
-