-
Anamwali Anzeru ndi OpusaNsanja ya Olonda—1990 | April 15
-
-
“Pakati pa usiku panali kufuula, Onani, mkwati! tulukani kukakomana naye. Pomwepo anauka anamwali onse amenewo, nakonza nyali zawo. Ndipo opusa anati kwa ochenjera, Tipatseniko ena a mafuta anu; chifukwa nyali zathu zirikuzima. Koma ochenjera anayankha nati, Kapena sangakwanire ife ndi inu; koma makamaka mukani kwa ogulitsa malonda, mukadzigulire inu nokha.”
Mafutawo akuphiphiritsira chija chimene chimakhalitsa Akristu owona kuwala monga zowunikira, ndicho, Mawu ouziridwa a Mulungu, pa amene akugwira mwamphamvu, pamodzi ndi mzimu woyera, umene umawathandiza kumvetsetsa Mawuwo. Mafuta auzimu amakhozetsa kagulu ka anamwali ochenjera kuunikira polandira mkwati pamene akupita ku phwando la ukwati. Koma gulu la anamwali opusa alibe mwa iwo, m’nsupa zawo, mafuta auzimu ofunikira. Chotero Yesu akulongosola zimene zikuchitika:
-
-
Anamwali Anzeru ndi OpusaNsanja ya Olonda—1990 | April 15
-
-
Pambuyo pa kufika kwa Kristu mu Ufumu wake wakumwamba, kagulu ka anamwali ochenjera ka Akristu odzozedwa enieni kanagalamukira ku mwaŵi wawo wapadera wa kuwunikira m’dziko lino lamdima m’chitamando cha kubweranso kwa Mkwati. Koma aja ochitiridwa chithunzi ndi anamwali opusa anali osakonzekera kupereka chitamando cholonjera chimenechi. Chotero pamene nthaŵi ifika, Kristu sakuwatsegulira khomo lopita ku phwando laukwati kumwamba. Iye akuwasiya kunja ku mdima wadziko wa ndiwe yani, kuti awonongeke limodzi ndi onse ochita kusayeruzika. Yesu akumaliza kuti: “Chifukwa chake dikirani, pakuti simudziŵa tsiku lake, kapena nthaŵi yake.” Mateyu 25:1-13.
-