-
Kuunika Kaamba ka “Mapeto a Dongosolo la Zinthu”Chisungiko cha Padziko Lonse mu Ulamuliro wa “Kalonga wa Mtendere”
-
-
13. Kodi ndimotani mmene anamwali ochenjera anayankhira pempho la anamwali opusa?
13 Tsopano, bwanji, za kagulu ka anamwali opusa? Yesu akupitirizabe kunena kuti: “Opusa anati kwa ochenjera, Tipatseniko ena a mafuta anu; chifukwa nyali zathu zirinkuzima. Koma ochenjera anayankha nati, Kapena sangakwanire ife ndi inu; koma makamaka mukani kwa ogulitsa malonda, mukadzigulire inu nokha.”—Mateyu 25:8, 9.
-
-
Kuunika Kaamba ka “Mapeto a Dongosolo la Zinthu”Chisungiko cha Padziko Lonse mu Ulamuliro wa “Kalonga wa Mtendere”
-
-
15. (a) Pamene nyengo ya mtendere inatseguka, kodi ndani pakati pa kagulu ka anamwali amene anayamba kusonyeza zikhoterero za kupusa kwauzimu? (b) Kodi nchifukwa ninji anamwali ochenjera anali osakhoza kuthandiza anamwali opusa mwauzimu?
15 Pamene nyengo ya mtendere inali kuyamba, ena a odzinenera kukhala atsamwali odzipatulira, obatizidwa anayamba kusonyeza kupusa kwauzimu. Pambuyo pa imfa ya prezidenti woyamba wa Watch Tower Society, Charles Taze Russell, iwo sanasonkhezeredwe mokwanira ndi kupita patsogolo kwauzimu kwa chipangizo chowoneka ndi maso cha Yehova Mulungu motsogozedwa ndi prezidenti wake watsopano, J. F. Rutherford. Kwenikweni mitima yawo siinali yogwirizana ndi njira imene zinthu zinali kuchitidwira. Iwo anasonyeza kupanda chiyamikiro ndi njira imene Yehova anali kuchitira ndi anthu ake. Motero, awo amene anali ofanana ndi anamwali ochenjera sakanakhoza kuloŵetsa mkhalidwe weniweni wa kupereka chichirikizo chochokera mu mtima kwa opusa ameneŵa amene anali kudzilekanitsa mowonjezerekawonjezereka.
16. Kodi kupusa kwauzimu kwa anamwali opusa kunawonekera motani?
16 Motero kupusa kwauzimu kunawonekera poyera. Motani? Mwa kulephera kukhala ndi mafuta ophiphiritsira panthaŵi zovutitsa pamene kuunika kwauzimu kunali kufunika kwakukulu pamene kupita patsogolo kwatsopano kunali kuchitika, kusonyeza kukhalako kwa Mkwati. Mwanjira yophiphiritsira inali nthaŵi yakuti munthuyo atuluke kukakomana naye ndi nyali yake itaunikidwa moŵala. Koma mmalo mwake, ofanana ndi anamwali opusa amenewo, amene nyali zawo zinali kuzima, anadzilekanitsa ndi ochenjera.
-