-
Kodi Nchiyani Chimakusonkhezerani Kutumikira Mulungu?Nsanja ya Olonda—1995 | June 15
-
-
17. M’mawu anuanu, simbani mwachidule fanizo la matalente.
17 Talingalirani za fanizo la Yesu la matalente, lolembedwa pa Mateyu 25:14-30. Munthu amene anali pafupi kuyenda ulendo wakutali anaitanitsa akapolo ake nawaikiza chuma chake. “Mmodzi anampatsa ndalama za matalente zisanu, ndi wina ziŵiri, ndi wina imodzi; kwa iwo onse monga nzeru zawo.” Kodi mbuyeyo anapezanji pamene anabwera kudzaŵerengera chuma ndi akapolo ake? Kapolo amene anapatsidwa matalente asanu anapindulanso ena asanu. Mofananamo, kapolo amene anapatsidwa matalente aŵiri anapindulanso ena aŵiri. Kapolo amene anapatsidwa talente limodzi analikwirira pansi ndipo sanachite nayo kalikonse kuti awonjezere chuma cha mbuyake. Kodi mbuyeyo anauona motani mkhalidwewo?
-
-
Kodi Nchiyani Chimakusonkhezerani Kutumikira Mulungu?Nsanja ya Olonda—1995 | June 15
-
-
19 Ndithudi, kapolo wachitatu sanayami kiridwe. Ndipo iye anaponyedwa kunja kumdima. Pokhala analandira talente limodzi chabe, sakanayembekezeredwa kubwezera zochuluka mofanana ndi kapolo wa matalente asanu. Komabe, iye sanayeseko nkomwe! Anapatsidwa chiweruzo choipa makamaka chifukwa cha mtima wake “woipa ndi waulesi,” umene unasonyeza kupanda kwake chikondi kwa mbuyake.
-