-
Chilungamo Osati Miyambo YapakamwaNsanja ya Olonda—1990 | October 1
-
-
18. (a) Kodi Ayuda anachisintha motani chilamulo chonena za kukonda mnansi wako, koma kodi Yesu analowereramo motani? (b) Kodi ndiliti limene linali yankho la Yesu kwa munthu wachilamulo wina amene anafuna kuika polekezera kugwiritsiridwa ntchito kwa “mnansi”?
18 M’chitsanzo chachisanu ndi chimodzi ndipo chomalizira, Yesu anasonyeza momvekera bwino mmene Chilamulo cha Mose chinafooketsedwera ndi miyambo ya arabi motere: “Munamva kuti kunanenedwa, Uzikondana ndi mnansi wako, ndi kumuda mdani wako: koma Ine ndinena kwa inu, Kondanani nao adani anu, ndi kupempherera iwo akuzunza inu.” (Mateyu 5:43, 44) Chilamulo cha Mose cholembedwa sichinaike polekezera chikondi: “Uzikonda mnansi wako monga udzikonda wekha.” (Levitiko 19:18) Anali Afarisi amene anatsekereza lamulo ili, ndipo m’kupatuka kwawo pa iyo iwo anaika polekezera liwu lakuti “mnansi” kwa anthu omwe anasunga miyamboyo. Zidatero kuti pamene Yesu pambuyo pake anakumbutsa wachilamulo wina za lamulo la ‘kukonda mnansi wanu monga inueni,’ munthuyo m’mawu ake anazemba motere: “Mnansi wanga ndani?” Yesu anamuyankha mwa kufotokoza fanizo la Msamariya wachifundo—dzipangeni nokha mnansi kwa okufunani.—Luka 10:25-37.
-
-
Chilungamo Osati Miyambo YapakamwaNsanja ya Olonda—1990 | October 1
-
-
20. Mmalo mwa kuchotsapo Chilamulo cha Mose, kodi ndimotani mmene Yesu anakulitsira ndi kuzamitsa mphamvu yake ndikuchikweza?
20 Chotero pamene Yesu analozera ku mbali za Chilamulo ndikuwonjezera kuti, “Koma Ine ndinena kwa inu,” sanali kuchotsa Chilamulo cha Mose ndikuchilowa mmalo ndi chinachake. Ayi, koma anali kuzamitsa ndi kukulitsa mphamvu yake mwa kusonyeza mzimu wokhala kumbuyo kwake. Chilamulo chapamwamba chaubale chimapereka chiweruzo chakuti wopitiriza kukhala ndi chidani ngwakupha. Chilamulo chapamwamba cha chiyero chimatsutsa kuti kupitiriza nawo maganizo okhumbira ndiko chigololo. Chilamulo chapamwamba chaukwati chimaletsa kusudzulana kwachinyengo kuti ndiko njira yotsogolera ku kukwatirananso kwachigololo. Chilamulo chapamwamba cha chowonadi chimasonyeza kuti kulapa kobwerezabwereza nkosayenera. Chilamulo chapamwamba cha kudekha chimaletsa kubwezera. Chilamulo chapamwamba cha chikondi chimafuna chikondi chaumulungu chomwe chiribe polekezera.
-