-
Asangalatsidwa ndi Mfarisi WotchukaNsanja ya Olonda—1988 | December 15
-
-
“Munthu wina anakonza phwando lalikulu, naitana anthu ambiri. Ndipo anatumiza kapolo wake . . . kukanena kwa oitanidwawo, ‘Idzani, chifukwa zonse zakonzeka tsopano.’ Ndipo onse ndi mtima umodzi anayamba kuwiringula. Woyamba anati kwa iye, ‘Ine ndagula munda ndipo ndiyenera ndituluke kukawuwona; ndikupempha, Undilole ine ndisafika.’ Ndipo anati wina, ‘Ine ndagula ng’ombe za magoli asanu, ndipo ndinka kukaziyesa; ndikupempha, Undilole ine ndisafika.’ Ndipo anati wina, ‘Ine ndakwatira mkazi, ndipo chifukwa chake sindingathe kudza.’”
-
-
Asangalatsidwa ndi Mfarisi WotchukaNsanja ya Olonda—1988 | December 15
-
-
Ndi mkhalidwe wotani umene ukulongosoledwa ndi fanizoli? Chabwino, “mbuye” wopereka chakudyayo akuimira Yehova Mulungu; “kapolo” wopereka chiitanoyo, Yesu Kristu; ndipo “phwando lamadzulo,” mwaŵi wa kukhala mu mzere kaamba ka Ufumu wa kumwamba.
-