Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Buku Limene Mungathe Kulikhulupirira—Gawo 6
    Galamukani!—2011 | April
    • M’Baibulo mulinso maulosi ofunika kwambiri amene analembedwa ndi kukwaniritsidwa pa nthawi ya ufumu wa Roma. Mwachitsanzo, pamene Yesu ankalowa mu Yerusalemu, analirira mzindawo ndipo analosera kuti asilikali a Roma adzauwononga. Iye ananena kuti: “Masiku adzakufikira pamene adani ako adzamanga mpanda wazisonga kukuzungulira. . . . Ndipo sadzasiya mwala pamwala unzake mwa iwe, chifukwa sunazindikire kuti nthawi yokuyendera inali itakwana.”—Luka 19:41-44.

  • Buku Limene Mungathe Kulikhulupirira—Gawo 6
    Galamukani!—2011 | April
    • Kodi kenako mzinda wa Yerusalemu unakumana ndi zotani? Asilikali a Roma anabwereranso ndipo pa nthawiyi ankatsogoleredwa ndi Vasipashani ndi mwana wake Tito. Iwo anali ndi asilikali okwana 60,000. Asilikaliwo analowa mumzindawo chikondwerero cha Pasika cha mu 70 C.E. chitatsala pang’ono kuyamba, ndipo anatsekereza anthu okhala mumzindawo komanso alendo amene anabwera kudzachita nawo chikondwererochi. Asilikali a Roma anagwetsa mitengo yambiri mumzindawo n’kumanga mpanda wazisonga, monga mmene Yesu ananenera. Patadutsa miyezi pafupifupi isanu, Aroma anagonjetsa mzindawo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena