Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lff phunziro 17
  • Kodi Yesu Ali Ndi Makhalidwe Otani?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Yesu Ali Ndi Makhalidwe Otani?
  • Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • FUFUZANI MOZAMA
  • ZOMWE TAPHUNZIRA
  • ONANI ZINANSO
  • Kodi Yesu Ndi Ndani?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • ‘Mwana Amakonda Kuululira Ena za Atate’
    Nsanja ya Olonda—2012
  • Kodi Yesu Khristu Ndi Ndani?
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Kodi Yesu Anachita Zotani Ali Padzikoli?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
Onani Zambiri
Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
lff phunziro 17
Phunziro 17. Yesu watambasula dzanja lake ndipo akuchiritsa mozizwitsa munthu yemwe akudwala.

PHUNZIRO 17

Kodi Yesu Ali Ndi Makhalidwe Otani?

Losindikizidwa
Losindikizidwa
Losindikizidwa

Tikamaphunzira zimene Yesu ananena ndi kuchita ali padziko lapansi, timapeza makhalidwe abwino kwambiri amene amachititsa kuti tizimukonda ndiponso kuti tizikonda Atate wake Yehova. Kodi ena mwa makhalidwe abwino kwambiri amene Yesu ali nawo ndi ati? Nanga tingamutsanzire bwanji?

1. Kodi Yesu amafanana ndi Atate wake m’njira ziti?

Kwa zaka mabiliyoni ambiri, Yesu anakhala kumwamba ndi Atate wake wachikondi. Kwa nthawi yonseyi, iye ankaona komanso kuphunzira zinthu zambiri kuchokera kwa Atate wake. Choncho iye amaganiza, kukhudzika ndi kuchita zinthu ngati Atate wake. (Werengani Yohane 5:19.) Ndipotu Yesu amatsanzira makhalidwe abwino amene Atate wake ali nawo. Mpake ananena kuti: “Amene waona ine waonanso Atate.” (Yohane 14:9) Mukamaphunzira makhalidwe a Yesu, mudzatha kumudziwa bwino Yehova. Mwachitsanzo, chifundo chomwe Yesu ankasonyeza anthu ndi umboni wakuti Yehova amakuderani nkhawa mukamavutika.

2. Kodi Yesu anasonyeza bwanji kuti amakonda Yehova?

Yesu anati: “Kuti dziko lidziwe kuti ndimakonda Atate, ndikuchita zinthu mogwirizana ndi zimene Atatewo anandilamula.” (Yohane 14:31) Yesu ali padziko lapansi, anasonyeza kuti amakonda kwambiri Atate wake powamvera ngakhale pamene zinali zovuta kuchita zimenezi. Iye ankakonda kulankhula zokhudza Atate wake ndipo ankathandiza anthu ena kuti nawonso ayambe kukonda Mulungu.​—Yohane 14:23.

3. Kodi Yesu anasonyeza bwanji kuti amakonda anthu?

Baibulo limasonyeza kuti Yesu amasangalala kwambiri ndi “mtundu wa anthu.” (Miyambo 8:31) Iye anasonyeza kuti amakonda anthu powalimbikitsa ndi kuwathandiza mosanyinyirika. Zodabwitsa zimene anachita zinkasonyeza kuti ali ndi mphamvu komanso zinkasonyeza kuti ndi wachifundo. (Maliko 1:40-42) Iye ankathandiza anthu mokoma mtima komanso mosakondera. Zomwe ankalankhula zinkatonthoza anthu a mtima wabwino amene ankamumvetsera komanso kuwathandiza kukhala ndi chiyembekezo. Yesu analolera kuvutika komanso kufa chifukwa amakonda anthu onse. Koma iye amakonda kwambiri anthu amene amakonda zimene ankaphunzitsa.​—Werengani Yohane 15:13, 14.

FUFUZANI MOZAMA

Fufuzani kuti mudziwe zambiri zokhudza makhalidwe a Yesu ndipo onani zimene mungachite kuti muzimutsanzira pa nkhani yosonyeza chikondi ndi kukhala opatsa.

4. Yesu amakonda Atate wake

Zimene Yesu ankachita zimatithandiza kudziwa zimene tingachite kuti tizikonda Mulungu. Werengani Luka 6:12 ndi Yohane 15:10 komanso 17:26. Mukawerenga lemba lililonse, kambiranani funso ili:

  • Potengera chitsanzo cha Yesu, tingasonyeze bwanji kuti timakonda Yehova?

Jesus praying.

Yesu ankakonda Atate wake akumwamba ndipo nthawi zambiri ankalankhula nawo m’pemphero

5. Yesu amaganizira anthu ovutika

Yesu ankaganizira kwambiri zofuna za anthu ena kuposa zofuna zake. Ankayesetsa kugwiritsa ntchito nthawi ndi mphamvu zake pothandiza anthu. Iye ankachita zimenezi ngakhale atatopa. Werengani Maliko 6:30-44, kenako mukambirane mafunso awa:

  • Munkhaniyi, kodi Yesu anachita zinthu ziti posonyeza kuti amaganizira ena?​—Onani vesi 31, 34, 41 ndi 42.

  • Kodi ndi khalidwe liti limene linachititsa kuti Yesu athandize anthuwo?​—Onani vesi 34.

  • Popeza kuti Yesu amatsanzira makhalidwe a Yehova, kodi zimenezi zikukuphunzitsani chiyani zokhudza Yehova?

  • Kodi ndi zinthu ziti zimene tingachite potsanzira Yesu pa nkhani yoganizira ena?

Yesu akudyetsa modabwitsa anthu masauzande ambiri pochulukitsa mikate 5 komanso nsomba zing’onozing’ono ziwiri. Kenako ophunzirawo anagawa chakudyacho kwa amuna, akazi ndi ana.

6. Yesu ndi wopatsa

Ngakhale kuti Yesu analibe zinthu zambiri zakuthupi, ankakonda kugawira ena zimene anali nazo. Iye amafuna kuti nafenso tizikhala opatsa. Werengani Machitidwe 20:35, kenako mukambirane funso ili:

  • Mogwirizana ndi zimene Yesu ananena, tizichita chiyani kuti tizikhala osangalala?

Onerani VIDIYO, kenako mukambirane funso ili:

VIDIYO: “Kupatsa Kumabweretsa Chimwemwe Chochuluka”​—Kachigawo Kake (4:00)

  • Kodi tingasonyeze bwanji mtima wopatsa ngakhale titakhala kuti tilibe zinthu zambiri?

Kodi mukudziwa?

Baibulo limatiphunzitsa kuti tizipemphera kwa Yehova m’dzina la Yesu. (Werengani Yohane 16:23, 24.) Tikamapemphera m’dzina la Yesu, timasonyeza kuti timayamikira zimene Yesu anachita potithandiza kuti Mulungu akhale mnzathu.

ANTHU ENA AMANENA KUTI: “Mulungu analemberatu zoti tizikumana ndi mavuto.”

  • Popeza kuti Yesu amatsanzira makhalidwe a Atate wake, kodi zimene ankachita zimasonyeza bwanji kuti si Yehova amene amachititsa kuti tizivutika?

ZOMWE TAPHUNZIRA

Yesu amakonda Yehova komanso amakonda anthu. Popeza kuti Yesu amatengera makhalidwe a Atate wake, mukadziwa zambiri zokhudza Yesu mudzamudziwanso bwino Yehova.

Kubwereza

  • Kodi tingasonyeze bwanji kuti timakonda Yehova ngati mmene Yesu ankachitira?

  • Kodi tingasonyeze bwanji kuti timakonda anthu ngati mmene Yesu ankachitira?

  • Ndi khalidwe liti la Yesu limene limakusangalatsani kwambiri?

Zoti Muchite

ONANI ZINANSO

Onani ena mwa makhalidwe a Yesu omwe tingatsanzire.

“Kuti Mutsanzire Yesu Muyenera . . .” (Yesu​—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo, tsamba 317)

Onani chifukwa chake tiyenera kupemphera kudzera m’dzina la Yesu.

“N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kupemphera M’dzina la Yesu?” (Nsanja ya Olonda, February 1, 2008)

Kodi Baibulo limanena chilichonse chokhudza mmene Yesu ankaonekera?

“Kodi Yesu Ankaoneka Bwanji?” (Nkhani yapawebusaiti)

Kodi tikuphunzirapo chiyani tikaona mmene Yesu ankachitira zinthu ndi akazi?

“Mulungu Amafuna Kuti Akazi Azilemekezedwa” (Nsanja ya Olonda, September 1, 2012)

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena