-
Anali Ngati Nthambi Zobala Zipatso Komanso Anali Mabwenzi a YesuYesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
-
-
“Nthambi iliyonse mwa ine yosabala zipatso [Atate wanga] amaidula, ndipo iliyonse yobala zipatso amaiyeretsa mwa kuitengulira kuti ibale zipatso zambiri. . . . Nthambi singabale zipatso payokha, pokhapokha ngati ndi yolumikizikabe kumpesawo. Chimodzimodzi inunso, simungabale zipatso mukapanda kukhala olumikizika kwa ine. Ine ndine mtengo wa mpesa, inu ndinu nthambi zake.”—Yohane 15:2-5.
-
-
Anali Ngati Nthambi Zobala Zipatso Komanso Anali Mabwenzi a YesuYesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
-
-
Yesu ananena kuti: “Amene ali wolumikizika kwa ine, inenso n’kukhala wolumikizika kwa iye, ameneyo amabala zipatso zochuluka, chifukwa simungathe kuchita kalikonse popanda ine.” Choncho otsatira okhulupirika a Yesu omwe anali ngati “nthambi” za mtengo wa mpesa, akanatha kubala zipatso zambiri potsanzira makhalidwe a Yesu, kulalikira za Ufumu wa Mulungu mwakhama komanso kuthandiza anthu ambiri kuti akhale ophunzira ake. Kodi chikanachitika n’chiyani ngati munthu akanasiya kugwirizana ndi Yesu komanso kubala zipatso? Yesu ananena kuti: “Ngati munthu sakhala wolumikizika kwa ine, amaponyedwa kunja.” Komanso Yesu ananena kuti: “Ngati mukhala ogwirizana ndi ine ndipo mawu anga akakhala mwa inu, mukhoza kupempha chilichonse chimene mukufuna ndipo chidzachitika kwa inu.”—Yohane 15:5-7.
-