-
Alephera Kumugwira IyeNsanja ya Olonda—1988 | April 15
-
-
M’kuyankha ku chiphunzitso cha Yesu, ena ayamba kunena kuti: “M’neneriyo ndi uyu ndithu,” mwachiwonekere akulozera kwa m’neneri wokulirapo kuposa Mose yemwe analonjezedwa kubwera. Ena akunena kuti: “Uyu ndi Kristu.” Koma ena akutsutsa: “Kodi Kristu adza kutuluka mu Galileya? Kodi sichinati chilembo kuti Kristu adza kutuluka mwa mbewu ya Davide, ndi kuchokera ku Betelehemu, ku mudzi kumene kunali Davide?”
-
-
Alephera Kumugwira IyeNsanja ya Olonda—1988 | April 15
-
-
Ngakhale kuti Malemba sanena mwachindunji kuti mneneri adzatuluka ku Galileya, iwo akulozadi kwa Kristu kukhala akuchokera kumeneko, akumanena kuti “kuwala kwakukulu” kudzawoneka m’gawo iri. Ndipo mosiyana ndi malingaliro olakwa, Yesu anabadwira mu Betelehemu, ndipo anali mbadwa ya Davide. Pamene kuli kwakuti Afarisi mwinamwake akudziwa za ichi, iwo mwachidziwikire ali ndi liwongo la kufalitsa malingaliro olakwa amene anthu ali nawo ponena za Yesu. Yohane 7:32-52; Yesaya 9:1, 2; Mateyu 4:13-17.
-