Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 11/02 tsamba 1
  • Lalikirani Choonadi Chonena za Yesu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Lalikirani Choonadi Chonena za Yesu
  • Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Nkhani Yofanana
  • “Njira Choonadi ndi Moyo”
    ‘Bwera Ukhale Wotsatira Wanga’
  • Uthenga Umene Tiyenera Kulengeza
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kutsatira “Khristu”?
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga
    Nsanja ya Olonda—1995
Onani Zambiri
Utumiki wathu wa Ufumu—2002
km 11/02 tsamba 1

Lalikirani Choonadi Chonena za Yesu

1 Akristu odzozedwa, mothandizana ndi anzawo a nkhosa zina, ali ndi ntchito yochitira ‘umboni za Yesu.’ (Chiv. 12:17) Imeneyi ndi ntchito yofunika kwambiri, chifukwa chakuti chipulumutso n’chotheka kudzera mwa Yesu yekhayo basi.—Yoh. 17:3; Mac. 4:12.

2 ‘Njira, Choonadi, ndi Moyo’: Yesu anati: “Ine ndine njira, ndi choonadi, ndi moyo. Palibe munthu adza kwa Atate, koma mwa Ine.” (Yoh. 14:6) Tingalankhule ndi Mulungu m’pemphero komanso tingakhale naye pa ubwenzi wabwino kudzera mwa Yesu yekha basi, amene ndi “njira.” (Yoh. 15:16) Yesu ndi “choonadi” chifukwa chakuti maulosi ndiponso zinthu za m’Malemba Achihebri zinakwaniritsidwa mwa iye. (Yoh. 1:17; Akol. 2:16, 17) Zoonadi, ntchito yeniyeni ya ulosi woona ndiyo kuunikira udindo wake waukulu pa kukwaniritsidwa kwa cholinga cha Mulungu. (Chiv. 19:10) Komanso, Yesu ndi “moyo.” Kuti onse apeze mphatso ya moyo wosatha, ayenera kukhulupirira nsembe ya dipo imene anapereka.—Yoh. 3:16, 36; Aheb. 2:9.

3 Mutu Komanso Mfumu Yolamulira: Anthu ayeneranso kuzindikira ulamuliro waukulu umene Yehova wapereka kwa Mwana wake. Yesu waikidwa kukhala Mfumu ya Ufumu wa Mulungu, amene ‘anthu ayenera kumumvera.’ (Gen. 49:10) Komanso, Yehova wamuika iye kukhala Mutu wa mpingo. (Aef. 1:22, 23) Tifunika kuthandiza anthu amene timaphunzira nawo Baibulo kudziŵa momwe Yesu amayang’anira mpingo ndiponso momwe amagwiritsira ntchito “kapolo wokhulupirika ndi wanzeru” kupereka “zakudya [zauzimu] panthaŵi yake.”—Mat. 24:45-47.

4 Mkulu wa Ansembe Wachifundo: Popeza kuti Yesu pamene anali padziko lapansi pano anakumana ndi mayesero ndi mavuto, “akhoza kuthandiza iwo amene ayesedwa.” (Aheb. 2:17, 18) N’zolimbikitsa kwambiri kwa anthu opanda ungwiro kudziŵa kuti Yesu amamva chifundo ndi zofooka zawo ndipo amawapempherera mwachikondi. (Aroma 8:34) Pa maziko a nsembe ya Yesu ndi mwa ntchito yake monga Mkulu wa Ansembe, tingalankhule ndi Yehova ‘molimbika mtima’ kuti tipeze ‘thandizo panthaŵi yakusoŵa.’—Aheb. 4:15, 16.

5 Kulimbikira kwathu kuuza ena choonadi chonena za Yesu kuwalimbikitsetu iwowo kuti nawonso amumvere ndi kum’tumikira.—Yoh. 14:15, 21.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena