Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • “Chifuniro cha Yehova Chichitike”
    ‘Kuchitira Umboni Mokwanira za Ufumu wa Mulungu’
    • Nkhaniyi yachokera pa Machitidwe 21:1-17

      1-4. N’chifukwa chiyani Paulo anayamba ulendo wopita ku Yerusalemu, nanga ankadziwa kuti akakumana ndi zotani?

      PAMENE Paulo ndi Luka ankasiyana ndi akulu a ku Efeso mumzinda wa Mileto, onse anamva chisoni. Zinali zovuta kwambiri kuti Paulo ndi Luka asiyane ndi abalewo, amene ankawakonda kwambiri. Amishonale awiriwo anakwera ngalawa, ndipo anatenga zinthu zofunikira pa ulendowo. Iwo analinso ndi mphatso zochokera m’mipingo yosiyanasiyana zoti akapereke kwa Akhristu osauka ku Yudeya ndipo ankafunitsitsa kuti mphatsozi zikafike kwa abalewo.

      2 Padoko laphokosoli pankaomba kamphepo kayaziyazi ndipo kenako ngalawayo inanyamuka. Paulo ndi Luka limodzi ndi anthu ena 7 amene ankayenda nawo pa ulendowo, ankayang’ana abale awo amene anaimirira m’mphepete mwa nyanja akuoneka achisoni. (Mac. 20:4, 14, 15) Paulo ndi anzakewo anapitiriza kubayibitsa abalewo mpaka ngalawayo inafika kutali moti sanathenso kuwaona.

  • “Chifuniro cha Yehova Chichitike”
    ‘Kuchitira Umboni Mokwanira za Ufumu wa Mulungu’
    • 5. Kodi Paulo ndi anzake anayenda bwanji kuti akafike ku Turo?

      5 Ngalawa imene Paulo ndi anzakewo anakwera ‘inayenda osakhota,’ kutanthauza kuti mphepo yabwino inkawakankha ndipo inawathandiza kuti akafike pachilumba cha Ko tsiku lomwelo. (Mac. 21:1) Zikuoneka kuti ngalawayo inagona kumeneko ndipo tsiku lotsatira inanyamuka n’kukafika ku Rode komanso ku Patara. Abalewo atafika ku Patara, doko limene linali chakum’mwera kwa Asia Minor, anakwera ngalawa yaikulu yonyamula katundu, ndipo sanaime paliponse mpaka anafika ku Turo, m’dera la Foinike. Ali m’njira, anadutsa pafupi ndi “chilumba cha Kupuro . . . kumanzere” kwa doko la pachilumbacho. (Mac. 21:3) N’chifukwa chiyani Luka, amene analemba buku la Machitidwe, anatchula mfundo imeneyi?

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena