-
“Mvetserani Mawu Anga Odziteteza”‘Kuchitira Umboni Mokwanira za Ufumu wa Mulungu’
-
-
11. Kodi akulu anapereka malangizo otani kwa Paulo, ndipo iye anafunika kuchita chiyani pomvera malangizowo? (Onaninso mawu a m’munsi.)
11 Akhristu a Chiyuda anakhumudwa kwambiri ngakhale kuti mphekesera zomwe anamvazo zinali zabodza. Choncho akulu anapatsa Paulo malangizo akuti: “Tili ndi amuna 4 amene anachita lumbiro. Utenge anthu amenewa ndipo ukachite nawo mwambo wa kudziyeretsa. Uwalipirire zonse zofunika, kuti amete tsitsi lawo. Ukatero, aliyense adziwa kuti mphekesera zimene anamva za iwe ndi nkhambakamwa chabe. Adzaona kuti ukuchita zinthu motsatira dongosolo komanso kuti umasunga Chilamulo.”c—Mac. 21:23, 24.
12. Kodi Paulo anasonyeza bwanji kuti anali womvera komanso wokonzeka kusintha, akulu a ku Yerusalemu atamupatsa malangizo?
12 Paulo akanatha kuuza akuluwo kuti vuto silinali mphekesera zimene anamvazo, koma Akhristu a Chiyudawo, amene ankaumirira kwambiri Chilamulo cha Mose. Koma iye anali wokonzeka kusintha bola ngati zimene anamuuzazo sizikanamuchititsa kuphwanya mfundo za Mulungu. M’mbuyomo, iye anali atalemba kuti: “Kwa anthu otsatira Chilamulo ndinakhala ngati wotsatira Chilamulo kuti ndithandize anthu otsatira chilamulo, ngakhale kuti sinditsatira Chilamulo.” (1 Akor. 9:20) Choncho pa nkhaniyi, Paulo anamvera akulu a ku Yerusalemu ndipo anakhala “ngati wotsatira Chilamulo.” Pamenepa iye anatipatsa chitsanzo chabwino masiku ano kuti tizimvera akulu ndiponso tisamaumirire kuchita zinthu mmene ifeyo tikufunira.—Aheb. 13:17.
Paulo ankagonjera ngati palibe chilichonse chosemphana ndi mfundo za m’Malemba. Kodi inunso mumatero?
-
-
“Mvetserani Mawu Anga Odziteteza”‘Kuchitira Umboni Mokwanira za Ufumu wa Mulungu’
-
-
c Akatswiri ena amanena kuti amunawo anachita lumbiro lokhala Anaziri. (Num. 6:1-21) N’zoona kuti Chilamulo cha Mose chimene chinali ndi mfundo zokhudza lumbiro limenelo chinali chitasiya kugwira ntchito. Komabe, Paulo ayenera kuti anaganiza kuti palibe cholakwika chilichonse ngati amunawo atachita zimene analumbira kwa Yehova. Choncho panalibe cholakwika kuti awalipirire zonse zofunika ndiponso kupita nawo limodzi. Sitikudziwa lumbiro limene anthuwo anachita. Komabe, zikuoneka kuti Paulo sakanawathandiza kuti apereke nsembe ya nyama (ngati mmene Anaziri ankachitira), chifukwa ankadziwa kuti nsembeyo singathandize munthu kukhala oyera ku machimo ake. Nsembe yangwiro ya Khristu inachititsa kuti nsembe za nyama zisakhalenso ndi mphamvu yochotsa machimo. Sitikudziwa zonse zimene Paulo anachita, komabe tikukhulupirira kuti sakanavomera kuchita chilichonse chosemphana ndi chikumbumtima chake.
-