-
Kulemekeza Ulamuliro Nkofunika kaamba ka Moyo WamtendereMtendere Weniweni ndi Chisungiko—Kodi Mungazipeze Motani?
-
-
11, 12. (a) Kodi ndimotani mmene malemba amasonyezera kuti pali ulamuliro wina woti ulingaliridwe? (b) Kodi mukanachitanji ngati olamulira adziko anaturutsa malamulo amene anawombana ndi zofuna za Mulungu, ndipo chifukwa ninji?
11 Komabe, Yesu anasonyeza kuti “Kaisara,” boma ladziko, sanali ulamuliro wokha woyenera kulingaliridwa. “Olamulira akulu” sali akulu kwa Mulungu ndiponso saali olingana naye. Mosemphana ndi zimenezo, iwo ali aang’ono kwambiri kwa iye. Chotero ulamuliro wawo ngwochepa, suli wotheratu. Chifukwa cha chimenechi, kaŵirikaŵiri Akristu ayang’anizana ndi chosankha chovuta. Chiri chosankha chimene inunso muyenera kuyang’anizana nacho. Pamene anthu okhala mu ulamuliro adzifunsilira zimene ziri za Mulungu, kodi mudzachitanji? Ngati iwo aletsa chimene Mulungu amalamula, kodi mudzamvera yani?
12 Atumwi a Yesu mwaulemu koma mwamphamvu analongosola kaimidwe kawo kuziŵalo za khoti lalikulu mu Yerusalemu kuti: “Weruzani, ngati nkwabwino pamaso pa Mulungu kumvera inu koposa Mulungu; pakuti sitingathe ife kuleka kulankhula zimene tinaziwona ndi kuzimva. . . . Tiyenera kumvera Mulungu koposa Anthu.” (Machitidwe 4:19, 20; 5:29) Nthawi zina maboma apereka ziletso m’nthawi zamaupandu, ndipo izi nzomvekera. Koma nthawi zina ziletso zaboma zingalinganizidwire kudodometsa kulambira kwathu Mulungu ndi kukupangitsa kukhala kosatheka kukwaniritsa mathayo operekedwa ndi Mulunguwo. Pamenepo chiyani? Mawu ouziridwa a Mulungu amayankha kuti: ‘Tiyenera kumvera Mulungu monga wolamulira koposa anthu’?
13, 14. (a) Kodi tiyenera kukhala osamalitsa motani kusakhala osamvera malamulo adziko kaamba ka zifukwa zathu chabe? (b) Kuchokera m’Malemba, sonyezani zifukwa za chimenechi.
13 Ngakhale kuli kwakuti kulemekeza thayo iri kwa Mulungu kungaombane ndi zimene “Kaisara,” amafuna, izi ziri zosiyana kwambiri ndi kuswa modzigangira malamulo amene sitimavomerezana nawo. Nzowona kuti, mwalingaliro lathu, malamulo ena angawonekere kukhala osafunika kapena oletsa mosayenera. Koma zimenezo sizimalungamitsa kunyalanyaza malamulo amene samaombana ndi malamulo a Mulungu. Bwanji ngati anthu onse anamvera kokha malamulo amene anawalingalira kukhala opindulitsa kwa iwo? Kukanachititsadi chipolowe.
-
-
Kulemekeza Ulamuliro Nkofunika kaamba ka Moyo WamtendereMtendere Weniweni ndi Chisungiko—Kodi Mungazipeze Motani?
-
-
[Chithunzi patsamba 134]
Atumwi a Yesu anauza khoti lalikulu kuti: “Tiyenera kumvera Mulungu koposa anthu”
-