Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • “Ife Tiyenera Kumvera Mulungu Monga Wolamulira”
    ‘Kuchitira Umboni Mokwanira za Ufumu wa Mulungu’
    • Banja likugwiritsa ntchito Baibulo komanso mabuku ofotokoza Baibulo polalikira kwa bambo amene waima panyumba yake.

      Mofanana ndi atumwi, ifenso timalalikira “kunyumba ndi nyumba”

      16. Kodi atumwi anasonyeza bwanji kuti ndi otsimikiza mtima kuchitira umboni mokwanira, ndipo ifeyo timatsanzira bwanji njira imene iwo ankagwiritsa ntchito polalikira?

      16 Atumwi sanachedwe kuyambiranso ntchito yawo yolalikira. Mopanda mantha, iwo “tsiku lililonse anapitiriza kuphunzitsa mwakhama m’kachisi ndiponso kunyumba ndi nyumba komanso ankalengeza uthenga wabwino wonena za Khristu Yesu.”d (Mac. 5:42) Atumwi amenewa, omwe ankalalikira mwakhama, anatsimikiza mtima kuchitira umboni mokwanira. Onani kuti iwo ankapita m’makomo a anthu kukalalikira uthenga wabwino potsatira zimene Yesu Khristu anawauza. (Mat. 10:7, 11-14) N’chifukwa chake anakwanitsa kudzaza Yerusalemu ndi mfundo zimene ankaphunzitsa. Masiku ano, Mboni za Yehova zimadziwika chifukwa chotsatira njira ya atumwi imeneyi polalikira. Tikamalalikira kunyumba ndi nyumba m’gawo lathu, timasonyeza kuti ifenso tikufuna kuonetsetsa kuti wina aliyense ali ndi mwayi woti amve uthenga wabwino. Kodi Yehova wadalitsa utumiki wathu wa kunyumba ndi nyumba? Inde. M’nthawi ya mapeto ino, anthu ambirimbiri akhala atumiki a Mulungu ndipo ambiri anamva koyamba za uthenga wabwino umenewu a Mboni atafika panyumba pawo.

      KULALIKIRA “KUNYUMBA NDI NYUMBA”

      Ngakhale kuti Khoti Lalikulu la Ayuda linaletsa ntchito yolalikira, ophunzira a Yesu “tsiku lililonse anapitiriza kuphunzitsa mwakhama m’kachisi ndiponso kunyumba ndi nyumba.” (Mac. 5:42) Koma kodi mawu akuti “kunyumba ndi nyumba” amatanthauza chiyani?

      M’Chigiriki, mawu akuti katʼ oiʹkon amatanthauza “kupita ku nyumba iliyonse.” Omasulira ambiri amanena kuti kugwiritsa ntchito mawu akuti ka·taʹ kukusonyeza kuti ophunzirawo ankalalikira nyumba ndi nyumba. Mawu akuti ka·taʹ anagwiritsidwanso ntchito palemba la Luka 8:1, limene limanena kuti Yesu analalikira “mumzinda ndi mzinda komanso mudzi ndi mudzi.”

      Palemba la Machitidwe 20:20 anagwiritsanso ntchito mawu omwewa koma osonyeza zinthu zambiri akuti katʼ oiʹkous. Palembali mtumwi Paulo anauza oyang’anira a Chikhristu kuti: “Sindinasiye kukuphunzitsani pagulu komanso kunyumba ndi nyumba.” Ena amaganiza kuti pamenepa Paulo ankanena za kuphunzitsa m’nyumba za akulu koma si choncho ndipo zimenezi zikuonekera bwino mu vesi lotsatira lomwe limati: “Koma ndachitira umboni mokwanira kwa Ayuda ndi kwa Agiriki omwe, kuti alape n’kubwerera kwa Mulungu komanso kuti ayambe kukhulupirira Ambuye wathu Yesu.” (Mac. 20:21) Okhulupirira anzake a Paulo anali atalapa kale ndipo ankakhulupirira Yesu. Choncho n’zoonekeratu kuti apa ankapita kunyumba ndi nyumba kukalalikira ndi kuphunzitsa anthu osakhulupirira.

  • “Ife Tiyenera Kumvera Mulungu Monga Wolamulira”
    ‘Kuchitira Umboni Mokwanira za Ufumu wa Mulungu’
Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena