-
Mpingo “Unayamba Kukhala Pamtendere”‘Kuchitira Umboni Mokwanira za Ufumu wa Mulungu’
-
-
1, 2. Kodi Saulo ankapita ku Damasiko kukatani?
ANTHU okwiya anali pa ulendo wopita kumzinda wa Damasiko kuti akachite zinthu zankhanza. Iwo ankafuna kuti akagwire, kumanga ndi kuzunza ophunzira a Yesu amene ankadana nawo kwambiri, kenako n’kupita nawo ku Khoti Lalikulu la Ayuda ku Yerusalemu kuti akawapatse chilango.
2 Saulo yemwe anali mtsogoleri wa anthuwo, anali kale ndi mlandu wamagazi.a Masiku angapo m’mbuyomu, pamene Ayuda ena ankhanza ankapha wophunzira wokhulupirika wa Yesu, Sitefano pomuponya miyala, Saulo ankaonerera ndipo anavomereza zimenezo. (Mac. 7:57–8:1) Kenako Saulo anayamba kuzunza Akhristu omwe ankakhala ku Yerusalemu. Koma sanasiyire pomwepa, anayamba kusakasaka ndiponso kuzunza Akhristu amene ankakhala m’madera enanso. Iye ankafuna kuthetseratu gulu la anthu limene ankaliona ngati losokoneza kwambiri, lomwe linkadziwika kuti “Njirayo.”—Mac. 9:1, 2; onani bokosi lakuti “Saulo Anali ndi Mphamvu Zomanga Akhristu ku Damasiko.”
-