-
‘Kodi Ndichitenji Kuti Ndipulumuke?’Nsanja ya Olonda—1989 | September 15
-
-
‘KODI ndichitenji kuti ndipulumuke?’ Funso limeneli linafunsidwa kalelo m’chaka cha 50 C.E. ndi wosunga ndende mu Filipi, Makedoniya. Panali patangochitika chivomezi chachikulu, ndipo makomo andende imene anali kuyang’anira anatseguka. Akumaganiza kuti andendewo athaŵa, wosunga ndendeyo anali pafupi kudzipha. Koma mmodzi wa andendewo, mtumwi Paulo, anafuula kuti: “Usadzipweteka wekha; tonse tiri muno.”—Machitidwe 16:25-30.
Paulo ndi wandende mnzake, Sila, anali atabwera ku Filipi kudzalalikira uthenga wa chipulumutso, ndipo iwo anali m’ndende chifukwa cha zinenezo zabodza zotsutsana nawo. Akumayamikira kuti andendewo sanathaŵe, wosunga ndendeyo anafuna kumva uthenga wa Paulo ndi Sila. Kodi nchiyani chimene iye akafunikira kuchita kuti apeze chipulumutso cholalikidwa ndi amishonale Achikristu aŵiri amenewa?
-
-
‘Kodi Ndichitenji Kuti Ndipulumuke?’Nsanja ya Olonda—1989 | September 15
-
-
Mmenemo simmene zinaliri pamene Akristu a m’zaka za zana loyamba anapeza chipulumutso. Wosunga ndende wa ku Filipi ‘sanatseke maganizo ake’ pamene mtumwi Paulo anayankha funso lake lakuti, ‘Kodi ndichitenji kuti ndipulumuke?’ Ndipo Paulo ndi Sila sanalinganize ‘kuwukira malingaliro ake’ ndi kupempha chopereka cha ndalama chachikulu. M’malomwake, “anamuuza iye mawu a [Yehova, NW].” Akumalingalira ndi munthuyo, iwo anamthandiza kumvetsetsa bwino makonzedwe a Mulungu kaamba ka chipulumutso.—Machitidwe 16:32.
-