-
Nkwandani Komwe Tingayang’ane Kaamba ka Chilungamo Chowona?Nsanja ya Olonda—1989 | February 15
-
-
10. Ndimotani mmene Paulo anagwiritsira ntchito kuchenjera m’kudziŵikitsa chidziŵitso chake?
10 Onani kuchokera pa Machitidwe 17:22, 23 ndi luso ndi nzeru zimene Paulo anayamba nazo. Pamene iye anadziŵikitsa mmene anthu a ku Atene analiri opembedza ndi unyinji wa mafano amene anali nawo, ena a amvetseri ake angakhale anachitenga icho monga chiyamikiro. M’malo mwa kuwukira kukhulupirira kwawo mwa milungu yambiri, Paulo analunjikitsa chidwi pa guwa lansembe limene iye anawona, lomwe linaperekedwa “Kwa Mulungu Wosadziŵika.” Umboni wa mbiri yakale umasonyeza kuti maguwa ansembe oterowo analiko, chomwe chiyenera kulimbikitsa chidaliro chathu m’mbiri ya Luka. Paulo anagwiritsira ntchito guwa lansembe limeneli monga maziko. Anthu a ku Atene anakonda chidziŵitso ndi nzeru. Komabe, iwo anavomereza kuti panali mulungu yemwe kwa iwo anali “wosadziŵika” (Chigriki, aʹgno·stos). Chinali kokha chanzeru, chotero, kuti iwo alole Paulo kumulongosola iye kwa iwo. Palibe wina aliyense amene akanapeza cholakwika ndi kulingalira koteroko, kodi akanatero?
Kodi Mulungu Ngosadziŵika?
11. Ndi mwanjira yotani mmene Paulo anapangitsira gulu lake kulingalira ponena za Mulungu wowona?
11 Chabwino, kodi nchiyani chimene chinali “Mulungu wosadziŵika” ameneyu? “Mulunguyo” anapanga dziko ndi chirichonse chimene chiri mu ilo. Palibe munthu aliyense amene angakane kuti chilengedwe cha ponse ponse chiriko, kuti zomera ndi zinyama ziriko, kuti ife anthu tiripo. Mphamvu ndi luntha, inde, nzeru, zosonyezedwa m’zonsezi zimalozera ku kukhala kwake chotulukapo cha Mlengi wanzeru ndi wamphamvu, m’malo mwa mwaŵi. M’chenicheni, kugwirizana kwa Paulo kwa kulingalira kuli ngakhale koyenerera m’nthaŵi yathu.—Chibvumbulutso 4:11; 10:6.
-
-
Nkwandani Komwe Tingayang’ane Kaamba ka Chilungamo Chowona?Nsanja ya Olonda—1989 | February 15
-
-
Amuna inu a Atene, m’zinthu zonse ndiwona kuti muli akupembedzetsa. 23 Pakuti popita, ndi kuwona zinthu zimene muzipembedza, ndipezanso guwa la nsembe lolembedwa potere, KWA MULUNGU WOSADZIŴIKA. Chimene muchipembedza osachidziŵa, chimenecho ndichilalikira kwa inu. 24 Mulungu amene analenga dziko lapansi ndi zonse ziri momwemo, Iyeyo, ndiye [Ambuye, NW] mwini kumwamba ndi dziko lapansi, sakhala m’nyumba zakachisi zomangidwa ndi manja; 25 satumikidwa ndi manja a anthu, monga wosowa kanthu, popeza Iye mwini apatsa zonse moyo ndi mpweya ndi zinthu zonse; 26 ndipo ndi mmodzi analenga mitunu yonse ya anthu, kuti akhale ponse pa nkhope ya dziko lapansi, atapangiratu nyengo zawo, ndi malekezero a pokhala pawo; 27 kuti afunefune Mulungu, kapena akamfufuze ndi kumpeza, ngakhale sakhala patari ndi yense wa ife; 28 pakuti mwa Iye tikhala ndi moyo ndi kuyendayenda, ndi kupeza mkhalidwe wathu; monga enanso a akuyimba anu ati, Pakuti ifenso tiri mbadwa zake.
-