-
Timakhulupirira Kuti Anthu Amene Anamwalira AdzaukaNsanja ya Olonda (Yophunzira)—2020 | December
-
-
Yesu anali woyamba pa anthu onse amene anaukitsidwa kupita kumwamba (Onani ndime 15-16)b
15. Kodi “onse” amene ‘adzapatsidwe moyo’ akuphatikizapo ndani?
15 Onani kuti Paulo ananenanso kuti “mwa Khristu onse adzapatsidwa moyo.” (1 Akor. 15:22) Iye analembera kalatayi Akhristu odzozedwa a ku Korinto amene ankayembekezera kudzaukitsidwa n’kupita kumwamba. Akhristu amenewo ‘anayeretsedwa mwa Khristu Yesu ndi kuitanidwa kuti akhale oyera.’ Paulo anatchula za “anthu amene anagona mu imfa mwa Khristu.” (1 Akor. 1:2; 15:18; 2 Akor. 5:17) M’kalata yake ina analemba kuti ‘amene anagwirizana naye [Yesu] pokhala ndi imfa yofanana ndi yake,’ ‘adzagwirizananso naye poukitsidwa mofanana ndi iye.’ (Aroma 6:3-5) Yesu anaukitsidwa ndi thupi lauzimu ndipo anapita kumwamba. Zimenezi ndi zomwe zidzachitike kwa onse amene “ali ogwirizana ndi Khristu” kapena kuti Akhristu onse odzozedwa.
-
-
Timakhulupirira Kuti Anthu Amene Anamwalira AdzaukaNsanja ya Olonda (Yophunzira)—2020 | December
-
-
17. Kodi anthu amene “ali ogwirizana ndi Khristu” anayamba liti kuukitsidwa n’kupita kumwamba?
17 Pa nthawi imene Paulo ankalembera kalata Akhristu a ku Korinto, anthu amene “ali ogwirizana ndi Khristu” anali asanayambe kuukitsidwa n’kupita kumwamba. Paulo anasonyeza kuti zimenezi zidzachitika m’tsogolo. Iye anati: “Aliyense pamalo pake: Choyamba Khristu, amene ndi chipatso choyambirira, kenako ake a Khristu pa nthawi ya kukhalapo kwake.” (1 Akor. 15:23; 1 Ates. 4:15, 16) Panopa, tikukhala mu “nthawi ya kukhalapo” kwa Khristu imene Paulo ananenayi. Atumwi komanso Akhristu ena odzozedwa amene anamwalira ankafunika kuyembekezera nthawi ya kukhalapo imeneyi kuti alandire mphoto yawo yakumwamba ndi ‘kugwirizananso ndi Yesu poukitsidwa mofanana ndi iye.’
-