Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 3 | Yesetsani Kuchotsa Mtima Wachidani M’maganizo Mwanu
    Nsanja ya Olonda (Yogawira)—2022 | Na. 1
    • Baibulo Limati:

      “Sandulikani mwa kusintha maganizo anu, kuti muzindikire chimene chili chifuniro cha Mulungu, chabwino, chovomerezeka ndi changwiro.”—AROMA 12:2.

      Zimene Lembali Limatanthauza:

      Mulungu amadziwa bwino zimene timaganiza. (Yeremiya 17:10) Choncho pali zambiri zomwe tiyenera kuchita kuwonjezera pa kupewa kulankhula kapenanso kuchita zinthu zosonyeza kuti tili ndi mtima wachidani. Chidani chimayambira mumtima ndiponso m’maganizo athu ndiye n’chifukwa chake tiyenera kuthetseratu chidani mumtima komanso m’maganizo mwathu. Tikachita zimenezi m’pamenedi ‘tingasandulike’ komanso kuthetsa chidani.

  • 3 | Yesetsani Kuchotsa Mtima Wachidani M’maganizo Mwanu
    Nsanja ya Olonda (Yogawira)—2022 | Na. 1
    • N’chiyani chinathandiza Stephen kuti asiye khalidwe lachiwawa komanso lodana ndi anthu ena? Lemba lomwe linamuthandiza kwambiri ndi la Aroma 12:2. Iye anati: “Ndinazindikira kuti ndikufunika kusintha mmene ndimaganizira. Ndinafunika kusintha maganizo anga kuti ndizichita zinthu mwamtendere komanso kuona kuti kuchita zimenezi n’kofunika kwambiri pa moyo wanga.” Kwa zaka 40 tsopano, Stephen akukhala moyo wosangalala chifukwa anasiya kudana ndi anthu.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena