-
Akulu Achikhristu Ndi Antchito Anzathu Otipatsa ChimwemweNsanja ya Olonda—2013 | January 15
-
-
6, 7. (a) Kodi akulu angatsanzire bwanji Yesu, Paulo ndi atumiki ena a Mulungu? (b) N’chifukwa chiyani abale amasangalala tikamakumbukira mayina awo?
6 Abale ndi alongo athu ambiri amanena kuti amasangalala kwambiri akulu akamasonyeza kuti amawaganizira. Akulu akhoza kuchita zimenezi potengera chitsanzo cha Davide, Elihu ndiponso Yesu. (Werengani 2 Samueli 9:6; Yobu 33:1; Luka 19:5.) Atumiki a Yehova onsewa anasonyeza kuti amaganizira anthu ena powatchula mayina awo. Nayenso Paulo anadziwa kufunika kokumbukira ndiponso kugwiritsa ntchito mayina a Akhristu anzake. Pomaliza kalata yake ina, anapereka moni kwa abale ndi alongo oposa 25 ndipo anawatchula onse mayina awo. Mwachitsanzo anatchula Peresida, yemwe anali mlongo amene Paulo ananena za iye kuti: “Moni kwa Peresida, wokondedwa wathu.”—Aroma 16:3-15.
-
-
Akulu Achikhristu Ndi Antchito Anzathu Otipatsa ChimwemweNsanja ya Olonda—2013 | January 15
-
-
8. Kodi Paulo anatsatira chitsanzo cha Yehova ndi Yesu pa nkhani yofunika iti?
8 Paulo anasonyezanso kuti amaganizira ena powayamikira mochokera pansi pa mtima. Kuchita zimenezi kumapangitsanso Akhristu anzathu kukhala achimwemwe. M’kalata yomweyo, imene Paulo ananena kuti ankafunitsitsa kuthandiza abale ake kukhala achimwemwe, ananenanso kuti: “Ndimakunyadirani kwambiri.” (2 Akor. 7:4) Mawu amenewa ayenera kuti analimbikitsa kwambiri abale a ku Korinto. Paulo ananenanso mawu ngati amenewa m’makalata ake opita ku mipingo ina. (Aroma 1:8; Afil. 1:3-5; 1 Ates. 1:8) Paulo atatchula Peresida m’kalata yake yopita ku mpingo wa ku Roma, ananenanso za iye kuti: “Mayi ameneyu wachita ntchito zambiri potumikira Ambuye.” (Aroma 16:12) Mlongo wokhulupirika ameneyu ayenera kuti analimbikitsidwa kwambiri ndi mawuwa. Paulo ankatsatira chitsanzo cha Yehova ndiponso Yesu pa nkhani yoyamikira ena.—Werengani Maliko 1:9-11; Yohane 1:47; Chiv. 2:2, 13, 19.
-