Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kodi Kukhala Munthu Wauzimu Kumatanthauza Chiyani?
    Nsanja ya Olonda (Yophunzira)—2018 | February
    • KODI KUKHALA MUNTHU WAUZIMU KUMATANTHAUZA CHIYANI?

      3. Kodi Baibulo limafotokoza bwanji kusiyana pakati pa munthu wakuthupi ndi munthu wauzimu?

      3 Zimene mtumwi Paulo ananena zingatithandize kudziwa tanthauzo la munthu wauzimu. Iye anafotokoza kusiyana pakati pa “munthu wauzimu” ndi “munthu wakuthupi” kapena kuti “munthu wokonda zinthu za m’dziko.” (Werengani 1 Akorinto 2:14-16; mawu a m’munsi) Kodi anthu amenewa amasiyana bwanji? Paulo ananena kuti munthu wakuthupi “salandira zinthu za mzimu wa Mulungu, chifukwa amaziona ngati zopusa ndipo sangathe kuzidziwa.” Koma “munthu wauzimu” ndi amene “amafufuza zinthu zonse” ndipo ali ndi “maganizo a Khristu.” Paulo anatilimbikitsa kukhala anthu auzimu. Koma kodi munthu wakuthupi amasiyana ndi munthu wauzimu m’njira zinanso ziti?

  • Kodi Kukhala Munthu Wauzimu Kumatanthauza Chiyani?
    Nsanja ya Olonda (Yophunzira)—2018 | February
    • 6. Kodi munthu wauzimu tingamudziwe bwanji?

      6 Ndiye kodi kukhala munthu wauzimu kumatanthauza chiyani? Mosiyana ndi munthu wakuthupi, munthu wauzimu amaganizira kwambiri za ubwenzi wake ndi Mulungu. Amayesetsanso kuti ‘azitsanzira Mulungu.’ (Aef. 5:1) Apa tikutanthauza kuti amayesetsa kudziwa maganizo a Mulungu n’kumaona zinthu mmene Mulunguyo amazionera. Amadalira kwambiri Mulungu ndipo amayesetsa kutsatira mfundo zake pa zonse zimene amachita. (Sal. 119:33; 143:10) Munthu wotereyu sachita “ntchito za thupi” koma amakhala ndi “makhalidwe amene mzimu woyera umatulutsa.” (Agal. 5:22, 23) Kuti timvetse nkhaniyi tiyeni tiyerekezere chonchi: Munthu amene ali ndi luso pochita bizinezi anthu amangomunena kuti wabizinezi. N’chimodzimodzi ndi munthu amene amaganizira kwambiri zinthu zauzimu kapena kuti zokhudza kulambira Mulungu. Amatchedwa munthu wauzimu.

      7. Kodi Baibulo limati chiyani ponena za anthu auzimu?

      7 Yesu anasonyeza kuti anthu auzimu amakhala osangalala. Paja pa Mateyu 5:3 ananena kuti “Odala ndi anthu amene amazindikira zosowa zawo zauzimu, chifukwa ufumu wakumwamba ndi wawo.” Pofotokozanso za ubwino wokhala munthu wauzimu, lemba la Aroma 8:6 limanena kuti: “Kuika maganizo pa zinthu za thupi kumabweretsa imfa, koma kuika maganizo pa zinthu za mzimu kumabweretsa moyo ndi mtendere.” Munthu akamaika maganizo pa zinthu zauzimu amakhala pa mtendere ndi Mulungu, amakhala ndi mtendere mumtima komanso amakhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena