Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Khalani Ndi Chikondi Chimene Sichitha Konse
    Nsanja ya Olonda—2009 | December 15
    • 13. (a) Tchulani lemba la chaka cha 2010. (b) Kodi chikondi sichitha m’njira yotani?

      13 Kenako Paulo anafotokoza zimene chikondi chimachita ndi zimene sichichita. (Werengani 1 Akorinto 13:4-8.) Ndiyeno ganizirani ngati mumakwaniritsa zimene chikondi chimafuna. Kwenikweni muganizire mbali yomaliza ya vesi 7, ndi chiganizo choyamba cha vesi 8. Pamenepa pali mawu akuti: ‘Chikondi chimapirira zinthu zonse. Chikondi sichitha konse.’ Mawu amenewa ndi amene adzakhale lemba la chaka cha 2010. Onani kuti mu vesi 8, Paulo ananena kuti mphatso za mzimu, monga kunenera ndiponso kulankhula malilime, zimene Akhristu ankakhala nazo mpingo utangoyamba kumene, zidzatha. Sizidzakhalaponso. Koma chikondi sichidzatha. Yehova ndiye chimake cha chikondi, ndipo adzakhalako kosatha. Choncho, chikondi sichidzatha konse. Chidzakhalako kwamuyaya chifukwa ndi khalidwe la Mulungu wathu yemwenso adzakhalapo kwamuyaya.​—1 Yoh. 4:8.

  • Khalani Ndi Chikondi Chimene Sichitha Konse
    Nsanja ya Olonda—2009 | December 15
    • Chikondi Sichitha Konse

      20, 21. (a) Kodi chikondi n’chopambana kwambiri chifukwa chiyani? (b) N’chifukwa chiyani inuyo mukufunitsitsa kutsatira njira yopambana ya chikondi?

      20 Zimene zakhala zikuchitika pakati pa anthu a Yehova masiku ano, zikusonyezeratu kuti ndi nzeru ndithu kutsatira njira yopambana ya chikondi. Chikondi chimathandiza pa chilichonse. Taonani mmene Paulo anatsindikira mfundo ya choonadi imeneyi. Choyamba, iye ananena kuti mphatso za mzimu zidzatha mpingo wachikhristu ukadzakula. Ndipo anamaliza ndi mawu akuti: “Tsopano patsala zitatu izi: Chikhulupiriro, chiyembekezo, chikondi. Koma chachikulu pa zonsezi ndi chikondi.”​—1 Akor. 13:13

      21 Zinthu zimene timakhulupirira zikadzakwaniritsidwa, chikhulupiriro chathu pa zinthuzo chidzakhala chosafunika. Chiyembekezo chimene tili nacho pa malonjezo amene timalakalaka kuwaona atakwaniritsidwa, chidzatha zinthu zonse zikadzakhala zatsopano. Nanga kodi chikondi chidzathanso? Ayi sichidzatha, chidzakhalapo mpaka kalekale. Popeza tidzakhala ndi moyo wosatha, tidzaona ndiponso kumvetsa bwino mbali zosiyanasiyana zokhudza chikondi cha Mulungu. Choncho, mwa kuchita chifuniro cha Mulungu, chomwe ndi kutsatira njira yopambana ya chikondi chimene sichitha konse, mudzakhala ndi moyo kosatha.​—1 Yoh. 2:17.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena