-
Timakhulupirira Kuti Anthu Amene Anamwalira AdzaukaNsanja ya Olonda (Yophunzira)—2020 | December
-
-
12. Mogwirizana ndi 1 Petulo 3:18, 22, kodi kuukitsidwa kwa Yesu n’kosiyana bwanji ndi kuukitsidwa kwa anthu ena komwe kunachitika m’mbuyomu?
12 Paulo ankadziwa kuti Khristu “anaukitsidwa kwa akufa.” Kuukitsidwa kumeneku kunali kwapadera kuposa kwa anthu amene anaukitsidwa m’mbuyomu chifukwa patapita nthawi anthuwo anafanso. Paulo ananena kuti Yesu anali “chipatso choyambirira cha amene akugona mu imfa.” N’chifukwa chiyani ananena kuti Yesu anali chipatso choyambirira? Chifukwa choti anali woyamba kuukitsidwa ndi thupi lauzimu komanso anali woyamba kupita kumwamba.—1 Akor. 15:20; Mac. 26:23; werengani 1 Petulo 3:18, 22.
-
-
Timakhulupirira Kuti Anthu Amene Anamwalira AdzaukaNsanja ya Olonda (Yophunzira)—2020 | December
-
-
16. Kodi Paulo ankatanthauza chiyani pamene ananena kuti Yesu ndi “chipatso choyambirira”?
16 Paulo analemba kuti Khristu anaukitsidwa kwa akufa n’kukhala “chipatso choyambirira cha amene akugona mu imfa.” Kumbukirani kuti anthu ena ngati Lazaro anaukitsidwa n’kukhala ndi moyo padziko lapansi. Koma Yesu anali woyamba kuukitsidwa ndi thupi lauzimu n’kupatsidwa moyo wosatha. Tingamuyerekezere ndi zipatso zoyambirira kukolola zimene Aisiraeli ankapereka kwa Mulungu. Komanso ponena kuti Yesu ndi “chipatso choyambirira,” Paulo ankatanthauza kuti pambuyo pake anthu enanso adzaukitsidwa n’kupita kumwamba. Patapita nthawi atumwi ndi ena amene “ali ogwirizana ndi Khristu,” anaukitsidwa n’kupita kumwamba mofanana ndi Yesu.
-