-
‘Imfa Idzathetsedwa’Nsanja ya Olonda—1998 | July 1
-
-
10 “Chimaliziro” ndicho chimaliziro cha Ulamuliro wa Kristu wa Zaka Chikwi, pamene Yesu modzichepetsa ndi mokhulupirika akukapereka Ufumu kwa Mulungu ndi Atate wake. (Chivumbulutso 20:4) Chifuno cha Mulungu cha ‘kusonkhanitsa pamodzi zonse mwa Kristu’ chidzakhala chitakwaniritsidwa. (Aefeso 1:9, 10) Komabe, choyamba Kristu adzaphwanya “chiweruzo chonse, ndi ulamuliro wonse, ndi mphamvu yomwe” zotsutsana ndi chifuno cha Uchifumu wa Mulungu. Zimenezi zimaposa chiwonongeko cha pa Armagedo. (Chivumbulutso 16:16; 19:11-21) Paulo anati: “[Kristu] ayenera kuchita ufumu kufikira ataika adani onse pansi pa mapazi ake. Mdani wotsiriza amene adzathedwa ndiye imfa.” (1 Akorinto 15:25, 26) Inde, zotsalira zonse za uchimo wa Adamu ndi imfa zidzakhala zitachotsedwa. Choncho chimene chidzakhala chofunika nchakuti Mulungu adzasiya “manda” ali opanda kanthu mwa kuukitsamo akufawo.—Yohane 5:28.
-
-
‘Imfa Idzathetsedwa’Nsanja ya Olonda—1998 | July 1
-
-
15. Kodi zikutanthauzanji kuti oukitsidwawo ‘adzaweruzidwa mwa zolembedwa m’mabuku’?
15 Kodi ndi motani mmene anthu oukitsidwawo ‘adzaweruzidwira mwa zolembedwa m’mabuku, monga mwa ntchito zawo’? Mabuku ameneŵa si kaundula wa zochita zawo zakale; pamene anafa, iwo anamasulidwa kumachimo amene anachita ali ndi moyo. (Aroma 6:7, 23) Komabe, anthu oukitsidwawo adzakhalabe ndi uchimo wa Adamu. Ndiye kuti mabuku ameneŵa ayenera kuti adzakhala ndi malangizo aumulungu akuti onse azitsatira kuti apindule ndi nsembe ya Yesu Kristu mokwanira. Pamene uchimo wa Adamu wachotsedweratu, ‘imfa idzathetsedweratu.’ Pamene zaka chikwi zidzafika kumapeto, Mulungu adzakhala “zonse mu zonse.” (1 Akorinto 15:28) Munthu sadzafunikiranso chithandizo cha Mkulu wa Ansembe kapena Moombolo. Anthu onse adzakhala atabwezeretsedwa kuungwiro umene Adamu anasangalala nawo poyambirira.
-