-
Lino Ndilo Tsiku la Chipulumutso!Nsanja ya Olonda—1998 | December 15
-
-
12. Kodi ndi utumiki wofunika wotani umene akuuchita akazembe limodzi ndi nthumwi za Yehova?
12 Kuti tidzapulumuke, tiyenera kumvera mawu a Paulo, akuti: ‘Monga ochitira pamodzi [ndi Yehova] tidandauliranso kuti musalandire chisomo cha Mulungu kwachabe inu, pakuti anena, M’nyengo yolandiridwa ndinamva iwe, ndipo m’tsiku la chipulumutso ndinakuthandiza; taonani, tsopano ndiyo nyengo yabwino yolandiridwa, taonani, tsopano ndilo tsiku la chipulumutso.’ (2 Akorinto 6:1, 2) Akazembe odzozedwa a Yehova limodzi ndi nthumwi zake a “nkhosa zina,” salandira chisomo cha Mulungu kwachabe. (Yohane 10:16) Mwa khalidwe lawo labwino ndi khama lawo pochita utumiki wawo m’nyengo “yolandiridwa” ino, akufuna kuyanjidwa ndi Mulungu ndiponso akuuza anthu padziko lapansi kuti lino ndilo “tsiku lachipulumutso.”
-
-
Lino Ndilo Tsiku la Chipulumutso!Nsanja ya Olonda—1998 | December 15
-
-
15. Kodi Aisrayeli auzimu anayambira liti kuyesetsa kusonyeza kuti ngoyenerera chisomo cha Mulungu, ndipo ndi cholinga chotani?
15 Paulo anasonyeza kuti mawu a Yesaya 49:8 akugwira ntchito kwa Akristu odzozedwa, nawapempha kuti ‘asalandire chisomo cha Mulungu kwachabe’ mwa kulephera kukhala naye pamtendere panthaŵi “yolandiridwa” ndi kulephera kuyamikira “tsiku la chipulumutso” limene wapereka. Paulo anawonjezera kuti: “Taonani, tsopano ndiyo nyengo yabwino yolandiridwa, taonani, tsopano ndilo tsiku la chipulumutso.” (2 Akorinto 6:1-2) Chiyambire 33 C.E. pa Pentekoste, Aisrayeli auzimu akhala akuyesetsa kusonyeza kuti ngoyenerera chisomo cha Mulungu kotero kuti ‘nthaŵi yolandiridwayi’ kwa iwo ikhaledi “tsiku la chipulumutso.
-