-
Lino Ndilo Tsiku la Chipulumutso!Nsanja ya Olonda—1998 | December 15
-
-
12. Kodi ndi utumiki wofunika wotani umene akuuchita akazembe limodzi ndi nthumwi za Yehova?
12 Kuti tidzapulumuke, tiyenera kumvera mawu a Paulo, akuti: ‘Monga ochitira pamodzi [ndi Yehova] tidandauliranso kuti musalandire chisomo cha Mulungu kwachabe inu, pakuti anena, M’nyengo yolandiridwa ndinamva iwe, ndipo m’tsiku la chipulumutso ndinakuthandiza; taonani, tsopano ndiyo nyengo yabwino yolandiridwa, taonani, tsopano ndilo tsiku la chipulumutso.’ (2 Akorinto 6:1, 2) Akazembe odzozedwa a Yehova limodzi ndi nthumwi zake a “nkhosa zina,” salandira chisomo cha Mulungu kwachabe. (Yohane 10:16) Mwa khalidwe lawo labwino ndi khama lawo pochita utumiki wawo m’nyengo “yolandiridwa” ino, akufuna kuyanjidwa ndi Mulungu ndiponso akuuza anthu padziko lapansi kuti lino ndilo “tsiku lachipulumutso.”
13. Kodi mfundo yaikulu pa Yesaya 49:8 ndi iti, ndipo inakwanira bwanji?
13 Paulo ananena mawu a pa Yesaya 49:8, akuti: “Atero Yehova, nthawi yondikomera ndakuyankha Iwe, ndi tsiku la chipulumutso ndakuthandiza; ndipo ndidzakusunga ndi kupatsa Iwe ukhale pangano la anthu, kuti ukhazikitse dziko, nuwaloŵetse m’zoloŵa zopasuka m’malo abwinja.” Ulosi umenewu unakwanira choyamba pamene Aisrayeli anamasulidwa kuukapolo ku Babulo ndiyeno nkudzabwerera kudziko lawo labwinja.—Yesaya 49:3, 9.
14. Kodi Yesaya 49:8 anakwaniritsidwa motani kwa Yesu?
14 Ulosi wa Yesayawo, potsirizika kukwanira kwake, Yehova anapatsa “mtumiki” wake Yesu akhale ‘kuunika kwa amitundu, kuti [Mulungu] adzapulumutse anthu mpaka kumalekezero a dziko lapansi.’ (Yesaya 49:6, 8; yerekezerani ndi Yesaya 42:1-4, 6, 7; Mateyu 12:18-21.) Zikuoneka kuti ‘nthaŵi yokomera Yehova,’ kapena “nthaŵi yolandiridwa,” inafika pamene Yesu anali padziko lapansi. Anapemphera, ndipo Mulungu ‘anamyankha.’ Kwa Yesu, limenelo linalidi “tsiku la chipulumutso” chifukwa anakhulupirikabe moti “anakhala kwa onse akumvera Iye chifukwa cha chipulumutso chosatha.”—Ahebri 5:7, 9; Yohane 12:27, 28.
15. Kodi Aisrayeli auzimu anayambira liti kuyesetsa kusonyeza kuti ngoyenerera chisomo cha Mulungu, ndipo ndi cholinga chotani?
15 Paulo anasonyeza kuti mawu a Yesaya 49:8 akugwira ntchito kwa Akristu odzozedwa, nawapempha kuti ‘asalandire chisomo cha Mulungu kwachabe’ mwa kulephera kukhala naye pamtendere panthaŵi “yolandiridwa” ndi kulephera kuyamikira “tsiku la chipulumutso” limene wapereka. Paulo anawonjezera kuti: “Taonani, tsopano ndiyo nyengo yabwino yolandiridwa, taonani, tsopano ndilo tsiku la chipulumutso.” (2 Akorinto 6:1-2) Chiyambire 33 C.E. pa Pentekoste, Aisrayeli auzimu akhala akuyesetsa kusonyeza kuti ngoyenerera chisomo cha Mulungu kotero kuti ‘nthaŵi yolandiridwayi’ kwa iwo ikhaledi “tsiku la chipulumutso.
-
-
Lino Ndilo Tsiku la Chipulumutso!Nsanja ya Olonda—1998 | December 15
-
-
Dalirani Chipulumutso cha Yehova
20. (a) Kodi Paulo ankakhumba kwambiri chiyani, ndipo nchifukwa chiyani anafunikira kuchita zinthu mwachangu? (b) Kodi nchiyani chikuchitika tsiku lino la chipulumutso limene tikukhalamo?
20 Pamene Paulo analembera Akorinto kalata yake yachiŵiri cha m’ma 55 C.E., panali patangotsala zaka 15 kuti dongosolo lazinthu la Ayuda lithe. Mtumwiyo anakhumbadi kuti Ayuda ndi Akunja ayanjanenso ndi Mulungu kudzera mwa Kristu. Limenelo linali tsiku la chipulumutso, ndipo anafunikira kuchita zinthu mwachangu. Ifenso tili m’nyengo yofananayo ya mapeto a dongosolo lazinthu chiyambire 1914. Ntchito yapadziko lonse yolalikira Ufumu yomwe ikugwiridwa tsopano lino ikusonyeza kuti lino ndilodi tsiku la chipulumutso.
21. (a) Kodi ndi lemba liti limene lasinkhidwa kuti likhale lemba la chaka cha 1999? (b) Kodi tiyenera kukhala tikuchitanji tsiku lino la chipulumutso?
21 Anthu amitundu yonse afunikira kumva mmene Mulungu wakonzera njira yowapulumutsira kudzera mwa Yesu Kristu. Nthaŵi isawonongeke. Paulo analemba kuti: “Taonani, tsopano ndilo tsiku la chipulumutso.” Mawu amenewa a pa 2 Akorinto 6:2 adzakhala lemba lachaka cha 1999 la Mboni za Yehova. Nloyeneradi, chifukwa tatsala pang’ono kuona chiwonongeko choposa cha Yerusalemu ndi kachisi wake! Posachedwapa dongosolo lazinthu lonseli lidzatha, ndipo zidzakhudza aliyense padziko lapansi. Nthaŵi yochitapo kanthu ndiyo tsopano lino—osati maŵa. Ngati tikukhulupirira kuti amene amapulumutsa ndi Yehova, ngati timamkonda, ndipo ngati timaona moyo wosatha monga chinthu chopambana, sitidzalandira chisomo cha Mulungu pachabe. Mumtima mwathu ngati tikukhumbadi kulemekeza Yehova, tidzasonyeza mwa mawu ndi zochita zathu kuti tikunenetsadi tikamalengeza kuti: “Taonani, tsopano ndilo tsiku la chipulumutso.”
-