-
Kodi Muli ndi Mphamvu Iliyonse pa Tsogolo Lanu?Nsanja ya Olonda—2005 | January 15
-
-
Mtumwi Paulo analemba kuti: “[Mulungu] anatidalitsa ife ndi dalitso lonse la mzimu m’zakumwamba mwa Kristu; monga anatisankha ife mwa Iye, lisanakhazikike dziko lapansi . . . Anatikonzeratu tilandiridwe ngati ana a Iye yekha mwa Yesu Kristu.” (Aefeso 1:3-5) Kodi Mulungu anakonzeratu chiyani, ndipo kodi mawu akuti anawasankha “lisanakhazikike dziko lapansi” amatanthauza chiyani?
-
-
Kodi Muli ndi Mphamvu Iliyonse pa Tsogolo Lanu?Nsanja ya Olonda—2005 | January 15
-
-
Kodi Paulo ankanena za dziko liti pamene anati: “[Mulungu] anatisankha ife mwa Iye, lisanakhazikike dziko lapansi?” Dziko limene Paulo anali kunena apa si dziko limene Mulungu anayambitsa pamene analenga Adamu ndi Hava. Dziko limenelo ‘linali labwino,’ chifukwa linali lopanda uchimo ndiponso zoipa zilizonse. (Genesis 1:31) Motero silimafunikira kuti ‘liwomboledwe’ kuuchimo.—Aefeso 1:7.
Dziko limene Paulo ankanena apa ndi dziko limene linadzakhalapo Adamu ndi Hava ataukira Mulungu mu Edene ndipo limeneli ndi dziko losiyana kwambiri ndi dziko limene Mulungu ankafuna pachiyambi. Ndi dziko limene linayamba ana a Adamu ndi Hava atabadwa. Dziko limenelo ndi dziko la anthu amene anatalikirana kwambiri ndi Mulungu omwenso ali akapolo a uchimo ndi zoipa. Ndi dziko la anthu osachimwa mwadala monga Adamu ndi Hava chifukwa iwowa angathe kuwomboledwa.—Aroma 5:12; 8:18-21.
Yehova Mulungu anapezeratu njira yokonzera vuto limene linabuka chifukwa cha anthu awiri amene anaukira mu Edene aja. Atangoona kuti pakufunika bungwe lapadera, nthawi yomweyo iye anakonza zoti kudzakhale Ufumu wa Mesiya ndipo anauika m’manja mwa Yesu Kristu, komanso anakonza zoti adzagwiritsira ntchito Ufumuwu powombola anthu ku uchimo wa Adamu. (Mateyu 6:10) Mulungu anachita zimenezi “lisanakhazikike dziko lapansi” la anthu otha kuwomboledwa, kutanthauza kuti anachita zimenezi Adamu ndi Hava asanabale ana.
-