Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Musalekanitse Chimene Mulungu Anachimanga Pamodzi
    Nsanja ya Olonda—2007 | May 1
    • 13. Kodi m’Baibulo muli mfundo zotani zothandiza akazi?

      13 Baibulo lili ndi mfundo zothandizanso akazi. Lemba la Aefeso 5:22-24, 33 limati: “Akazi agonjere amuna awo monga kugonjera Ambuye, chifukwa mwamuna ndiye mutu wa mkazi wake monganso Khristu alili mutu wa mpingo, pokhala iye mpulumutsi wa thupilo. Ndipotu, monga mpingo umagonjera Khristu, akazinso agonjere amuna awo m’chilichonse. . . . Mkazi akhale ndi ulemu waukulu kwa mwamuna wake.”

  • Musalekanitse Chimene Mulungu Anachimanga Pamodzi
    Nsanja ya Olonda—2007 | May 1
    • 15. Kodi Baibulo lili ndi uphungu wotani kwa akazi?

      15 Paulo ananenanso kuti mkazi “akhale ndi ulemu waukulu kwa mwamuna wake.” Mkazi wachikhristu azikhala ndi “mzimu wabata ndi wofatsa,” ndipo asapikisane ndi mwamuna wake kapena kumangoyendera zake. (1 Petulo 3:4) Mkazi woopa Mulungu amalimbikira kugwira ntchito kuti athandize banja lake ndipo potero mwamuna wake amalemekezedwa. (Tito 2:4, 5) Amayesetsa kunena zabwino za mwamuna wake ndipo sachita chilichonse chimene chingamuchotsere ulemu. Amathandizanso mwamuna wake pa zimene wagamula kuti zitheke.​—Miyambo 14:1.

      16. Kodi akazi achikhristu angaphunzire chiyani kwa Sara ndi Rebeka?

      16 Sikuti mkazi wachikhristu akakhala ndi mzimu wabata ndi wofatsa ndiye kuti alibe mfundo kapena amaganiza moperewera. Kale, akazi oopa Mulungu, monga Sara ndi Rebeka, ananena maganizo awo ndipo Baibulo limasonyeza kuti Yehova anagwirizana nawo. (Genesis 21:8-12; 27:46–28:4) Akazi achikhristu nawonso ayenera kunena maganizo awo. Koma azichita zimenezi mwaulemu osati monyoza. Mkazi akamalankhula maganizo ake mwaulemu, mwamuna amasangalala ndipo amamvetsera.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena