-
Mmene Mungadziŵire ndi Kuthetsera Chofooka Chilichonse ChauzimuNsanja ya Olonda—1999 | April 15
-
-
Kumenya nkhondo yauzimu—nkhondo yoloŵetsapo kulamulira maganizo ndi mtima wa Mkristu—tiyenera kuchita zonse zimene tingathe kuti titchinjirize maganizo athu. Kumbukirani kuti pakati pa zovala zauzimu za nkhondo pali “cha pachifuŵa cha chilungamo,” chimene chimateteza mtima wathu, ndi “chisoti cha chipulumutso,” chimene chimateteza maganizo athu. Kuphunzira kugwiritsa ntchito bwino zogaŵira zimenezi n’kumene kungatipezetse chipambano m’malo mogonja.—Aefeso 6:14-17; Miyambo 4:23; Aroma 12:2.
-
-
Mmene Mungadziŵire ndi Kuthetsera Chofooka Chilichonse ChauzimuNsanja ya Olonda—1999 | April 15
-
-
Kuvala “chisoti cha chipulumutso” kumaphatikizapo kumaganizira kwambiri madalitso odabwitsa a m’tsogolo, osadzilola kusokonezedwa ndi kukongola ndi kusangalatsa kwa dzikoli. (Ahebri 12:1-3; 1 Yohane 2:16) Kukhala ndi malingaliro ameneŵa kudzatithandiza kuika zinthu zauzimu patsogolo m’malo mwa mapindu akuthupi kapena kudzipezera phindu. (Mateyu 6:33) Choncho, pofuna kutsimikizira kuti tavala bwino chovala cha nkhondo chimenechi, moona mtima tiyenera kudzifunsa kuti: Kodi ndikulondola chiyani m’moyo? Kodi ndili ndi zolinga zauzimu zenizeni? Kodi ndikutani pofuna kuzikwaniritsa? Kaya ndife otsalira mwa Akristu odzozedwa kapena a mu “khamu lalikulu,” tiyenera kutsanzira Paulo, amene anati: “Ine sindiŵerengera ndekha kuti ndatha kuchigwira: koma chinthu chimodzi ndichichita; poiŵaladi zam’mbuyo, ndi kutambalitsira zam’tsogolo, ndilondetsa polekezerapo.”—Chivumbulutso 7:9; Afilipi 3:13, 14.
-