Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mungatani Kuti Musasiye Kuphunzira Baibulo?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 4. Muziona kuti kuphunzira Baibulo n’kofunika kwambiri

      Nthawi zina anthufe timatanganidwa kwambiri moti zingaoneke ngati n’zosatheka kupeza nthawi yophunzira Baibulo. Kodi n’chiyani chingatithandize? Werengani Afilipi 1:​10, kenako mukambirane mafunso awa:

      • Kodi mumaona kuti ndi zinthu ziti zimene zili m’gulu la “zinthu zofunika kwambiri” pa moyo?

      • Mungatani kuti muziona kuti kuphunzira Baibulo ndi chinthu chofunika kwambiri pa moyo wanu?

      A. Zithunzi: Zithunzi zosonyeza kuika miyala ndi mchenga m’chitini. 1. Mulu wa mchenga ndiponso wa miyala ikuluikulu. 2. Chitini chatsala pang’ono kudzadza ndi mchenga. 3. Miyala ikuluikulu ili pamwamba pa mchenga ndipo ina yagwera pansi. B. Zithunzi: 1. Mulu womwe uja wa mchenga komanso wa miyala. 2. Chitini chomwe chija chatsala pang’ono kudzaza ndi miyala ikuluikulu. 3. Mchenga wathiridwa m’chitini ndipo wadzaza kufika kukamwa. Mchenga wochepa uli pansi.
      1. Ngati mungayambe kuika mchenga m’chitini pambuyo pake n’kuika miyala, miyalayo singakwanemo yonse

      2. Ngati mungayambe kuika miyala m’chitinimo sizingavute kuti mchenga wambiri ulowemo. N’chimodzimodzinso ndi zimene zimachitika mukaika zinthu zofunika kwambiri pamalo oyamba m’moyo wanu. Mumatha kuzikwaniritsa komanso mumapeza nthawi yochitira zinthu zina

      Tikamaphunzira Baibulo timakhala tikudzidyetsa mwauzimu chifukwa chozindikira kuti tikufunikira kudziwa Mulungu ndi kumulambira. Werengani Mateyu 5:​3, kenako mukambirane funso ili:

      • Kodi timapindula bwanji tikamayesetsa kupeza nthawi yophunzira Baibulo?

  • Muzisankha Zosangalatsa Zomwe Sizingakhumudwitse Yehova
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 4. Muzigwiritsa ntchito nthawi yanu mwanzeru

      Onerani VIDIYO, kenako mukambirane funso ili:

      VIDIYO: Kodi Mumagwiritsa Ntchito Bwanji Nthawi Yanu? (2:45)

      • Ngakhale kuti m’bale wamuvidiyoyi sankaonera zinthu zoipa, kodi vuto lake linali lotani?

      Werengani Afilipi 1:10, kenako mukambirane funso ili:

      • Kodi vesili lingatithandize bwanji kupewa kuthera nthawi yaitali pa zinthu zosangalatsa?

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena