Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Anadedwa Chifukwa cha Chikhulupiriro Chawo
    Nsanja ya Olonda—1998 | December 1
    • 17. Kodi nchiyani chikusonyeza kuti ntchito yolalikira ya Akristu a m’zaka za zana loyamba inali yogwira mtima?

      17 Akristu a m’zaka za zana loyamba analalikira uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu ndi changu chosaneneka. (Mateyu 24:14) Pofika cha m’ma 60 C.E., Paulo anatha kunena kuti uthenga wabwino ‘unalalikidwa cholengedwa chonse cha pansi pa thambo.’ (Akolose 1:23) Pofika kumapeto kwa zaka za zana loyamba, otsatira a Yesu anali atapanga ophunzira mu Ufumu wonse wa Roma​—ku Asia, ku Ulaya, ndi ku Afirika! Ngakhale anthu ena “a banja la Kaisara” anakhala Akristu.a (Afilipi 4:22) Kulalikira mwachangu kumeneku kunadzutsa mkwiyo. Neander anati: “Chikristu chinafalikira bwino pakati pa anthu a udindo uliwonsewo, ndipo chinaoneka kuti chidzaposa chipembedzo cha m’dzikomo.”

  • Anadedwa Chifukwa cha Chikhulupiriro Chawo
    Nsanja ya Olonda—1998 | December 1
    • a Mawu akuti “banja la Kaisara” sanena kwenikweni za anthu amene anali abale ake enieni a Nero, yemwe anali kulamulira panthaŵiyo. M’malo mwake, anganene za antchito ake a panyumba ndi maofesala ang’onoang’ono, amene mwinamwake anali kugwira ntchito zonga ngati kuphika ndi kusamalira panyumba m’malo mwa banja lachifumulo ndi antchito awo ena.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena