Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Zimene Mungachite Kuti Muziuzako Ena Uthenga Wabwino
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 1. Mungatani kuti muziuzako anthu amene mukuwadziwa zinthu zomwe mwaphunzira?

      Ophunzira a Yesu ananena kuti: “Ife sitingaleke kulankhula zinthu zimene tinaziona ndi kuzimva.” (Machitidwe 4:20) Uwu ndi umboni wakuti ankakonda kwambiri choonadi ndipo ankafuna kuuza aliyense zokhudza choonadicho. Kodi ndi mmene inunso mukumvera? Ngati ndi choncho, ganizirani mipata imene mungaigwiritse ntchito kuti muuzeko achibale ndi anzanu zimene mwaphunzira, koma mwaulemu.​—Werengani Akolose 4:6.

      Mmene mungayambire

      • Mukamacheza ndi wachibale mukhoza kumuuzako mfundo inayake ya m’Baibulo ndipo munganene kuti: “Mlungu uno ndaphunzira mfundo inayake yosangalatsa.”

      • Ngati muli ndi mnzanu winawake amene akudwala kapena ali ndi nkhawa, mungamuuzeko lemba lolimbikitsa.

      • Anzanu akuntchito akakufunsani mmene moyo wanu ukuyendera, mungawauzeko zimene mwaphunzira pa phunziro la Baibulo kapena pamisonkhano ya mpingo.

      • Aonetseni anzanu webusaiti ya jw.org.

      • Mungapemphe anzanu kuti akhale nawo pamene mukuphunzira Baibulo kapena mungawaonetse mmene angapemphere munthu woti aziphunzira nawo pa jw.org.

  • Zimene Mungachite Kuti Muziuzako Ena Uthenga Wabwino
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 4. Muzichita zinthu mwaulemu

      Mukamalalikira uthenga wabwino musamangoganizira zimene mukufuna kunena, koma muziganiziranso mmene mungazinenere. Werengani 2 Timoteyo 2:24 ndi 1 Petulo 3:15, kenako mukambirane mafunso otsatirawa:

      • Kodi mungagwiritse ntchito bwanji mfundo za m’mavesiwa pokambirana ndi anthu zokhudza Baibulo?

      • Mwina achibale anu kapena anzanu angakutsutseni. Ndiye kodi muyenera kuchita chiyani? Nanga simukuyenera kuchita chiyani?

      • N’chifukwa chiyani muyenera kufunsa mafunso omwe angawathandize kunena maganizo awo, m’malo mongowauza zoyenera kukhulupirira?

      Wophunzira Baibulo akuuza wachibale wake mfundo ina ya m’Baibulo.
Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena