Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Dziko Lapansi Silinayenera Iwo
    Nsanja ya Olonda—1987
    • 7. (a) Ndi ndani amene “mwa chikhulupiriro anagonjetsa maufumu omwe anali kulimbana nawo”?(b) Ndi ndani amene “anakwaniritsa chilungamo” mwa chikhulupiriro?

      7 Ndi chikhulupiriro mwachipambano tingakumane ndi chiyeso chiri chonse chaumphumphu ndipo tingakwaniritse chiri chonse m’chigwirizano ndi chifuno chaumulungu. (Werengani Ahebri 11:33, 34.) Mu Kulozera ku zochitika za chikhulupiriro zowonjezereka, mwachiwonekere Paulo anali kulingalira za oweruza, mafumu, ndi aneneri Achihebri, popeza iye anali atagotchula kumene anthu amene wo. “Mwachikhulupiriro” oweruza monga ngati Gideoni ndi Yefita “anagonjetsa maufumu omwe anali kulimbana nawo.” Chimodzimodzinso Mfumu Davide, yemwe anagonjetsa Afilisti, Amoabu, Asuri, a Edomu, ndi ena. (2 Samueli 8:1-14) Ndiponso mwachikhulupiriro, oweruza olungama “anakhazikitsa chilungamo,” ndipo uphungu wolungama wa Samueli ndi aneneri ena unafulumiza chifupifupi kupewa kapena kusiya kupanga choipa.​—1 Samueli 12: 20-25; Yesaya 1:10-20.

  • Dziko Lapansi Silinayenera Iwo
    Nsanja ya Olonda—1987
    • 10. Ndani amene “analaka mphamvu yamoto” mwa chikhulupiriro, ndipo kodi nchiyani chomwe chikhulupiriro chofananacho chidzatithandiza ife kuchita?

      10 Osunga umphumphu anzake a Danieli Achihebri Sadrake, Mesake, ndi Abedinego muchenicheni “analaka mphamvu ya moto.” Pamene anaopsezedwa ndi imfa m’ng’anjo yotentha kwambiri yamoto, iwo anauza Mfumu Nebukadinezara kuti, kaya Mulungu wawo akawapulumutsa iwo kapena ayi, iwo sadzatumikira milungu yake kapena kulambira fano lagolidi analiika. Yehova sanauzimitse moto m’ng’anjo imeneyo, koma anatsimikizira kuti siunawononge Ahebri atatu amenewo. (Danieli 3:1-30) Chikhulupiriro chofananacho chimatitheketsa ife kusunga umphumphu kulinga kwa Mulungu kumlingo wothekera angakhale ku imfa pamanja a adani.​—Chivumbulutso 2:10.

      11. (a) Mwa chikhulupiriro, ndani amene “anapulumuka nsonga ya lupanga”? (b) Ndani amene“analimbikitsidwa” mwa chikhulupiriro? (c) Ndi ndani amene “anakhala olimbamtima mu nkho ndo” ndi “kupitikitsa magulu ankhondo achilendo”?

      11 Davide “anapulumuka nsonga ya lupanga” ya amuna a Mfumu Sauli. (1 Samueli 19:9-17) Mneneri Eliya ndi Elisa nawonso anapulumuka imfa kuchoka ku lupanga. (1 Mafumu 19:1-3; 2 Mafumu 6:11-23) Koma ‘ndani amene kuchokera ku mkhalidwe wofooka analimbikitsidwa mwa chikhulupiriro’? Chabwino, Gideoni ana dzilingalira iye mwini ndi amuna ake kukhala ofooka kwambiri kupulumutsa Aisrayeli kuchoka kwa Amidyani. Koma iye “analimbikitsidwa” ndi Mulungu, yemwe anamupatsa chipambano​—ndipo ndi amuna 300 okha. (Oweruza 6:14-16; 7:2-7 22) “Kuchoka ku mkhalidwe wofooka” pamene tsitsi lake linametedwa, Samsoni “analimbikitsidwa” ndi Yehova ndi kubweretsa imfa pa Afilisti ambiri. (Oweruza 16:19-21, 28-30; yerekezani ndi Oweruza 15:13-19. ) Paulo angakhale atalingaliranso za Mfumu Hezekiya yemwe “analimbikitsidwa” kuchokera ku mkhalidwe wofooka mwa nkhondo ndipo angakhale mwakuthupi. (Yesaya 37:1-38:22) Pakati pa atumiki a Mulungu omwe “anakhala olimba mtima m’nkhondo” anali Woweruza Yefita ndi Mfumu Davide. (Oweruza 11:32, 33; 2 Samueli 22:1, 2, 30-38) Ndipo awo amene “anapitikitsa magulu ankhondo achilendo” anaphatikizapo Woweruza Baraki. (Oweruza 4:14-16) Zochitika zonsezi ziyenera kutitsimikizira ife kuti ndi chikhulupiriro tingapeze chipambano pa kukumanizana ndi chiyeso chamtundu uliwonse cha umphumphu wathu ndipo tingakwaniritse chiri chonse chomwe chiri m’chigwirizano ndi chifuno cha Yehova.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena