-
Zimene Baibulo Limanena pa Nkhani ya Ntchito Komanso NdalamaMungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
-
-
2. Kodi Baibulo limanena zotani pa nkhani zokhudza ndalama?
Baibulo limanena kuti ‘ndalama zimateteza.’ Komabe, limanenanso kuti ndalama sizingatithandize kukhala osangalala. (Mlaliki 7:12) M’pake kuti limatichenjeza kuti tisamakonde ndalama ndipo limatilimbikitsa kuti ‘tizikhutira ndi zimene tili nazo pa nthawiyo.’ (Werengani Aheberi 13:5.) Tikamakhala okhutira ndi zimene tili nazo, timapewa nkhawa zimene zimabwera chifukwa cha mtima wofuna kukhala ndi zinthu zambiri. Komanso timapewa ngongole zosafunikira. (Miyambo 22:7) Timapewanso mavuto amene amabwera chifukwa chotchova juga ndiponso kuchita nawo mabizinesi omwe amalimbikitsa anthu kulemera mwachangu.
-
-
Zimene Baibulo Limanena pa Nkhani ya Ntchito Komanso NdalamaMungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
-
-
5. Tikamakhutira ndi zimene tili nazo timakhala osangalala
Anthu ambiri amachita chilichonse chomwe angathe kuti apeze ndalama zambiri. Koma Baibulo silimatilimbikitsa kuchita zimenezi. Werengani 1 Timoteyo 6:6-8, kenako mukambirane funso ili:
Kodi Baibulo limatilimbikitsa kuchita chiyani?
Ngakhale titakhala ndi zinthu zochepa, tikhoza kumakhala osangalala. Onerani VIDIYO, kenako mukambirane funso lotsatirali.
N’chiyani chikupangitsa mabanjawa kukhala osangalala ngakhale kuti amapeza ndalama zochepa?
Kodi pangakhale vuto lotani ngati tili ndi zinthu zambiri koma tikufunanso kuwonjezera zina? Yesu ananena fanizo lomwe limasonyeza kuopsa kwa mtima umenewu. Werengani Luka 12:15-21, kenako mukambirane funso ili:
Kodi mwaphunzira zotani mufanizo la Yesuli?—Onani vesi 15.
Werengani Miyambo 10:22 ndipo muyerekezere ndi 1 Timoteyo 6:10. Kenako mukambirane mafunso awa:
Kodi mukuganiza kuti chofunika kwambiri n’chiyani, kukhala pa ubwenzi ndi Yehova kapena kukhala ndi ndalama zambiri? N’chifukwa chiyani mukutero?
Kodi munthu amene amangokhalira kufunafuna ndalama amakumana ndi mavuto otani?
-