-
Perekani Nsembe Zimene Zimakondweretsa YehovaNsanja ya Olonda—1989 | December 15
-
-
8. Kodi ndimotani mmene mukalongosolera mawu a Paulo pa Ahebri 13:9?
8 Kusasinthika kwaumunthu wa Yesu ndi ziphunzitso kuyenera kutipangitsa ife kumamatira ku chimene iye ndi atumwi ake anaphunzitsa. Ahebri anawuzidwa kuti: “Musatengedwe ndi maphunzitso amitundumitundu, ndi achilendo; pakuti nkokoma kuti mtima ukhazikike ndi chisomo; kosati ndi zakudya, zimene iwo adazitsata sanapindula nazo.”—Ahebri 13:9.
-
-
Perekani Nsembe Zimene Zimakondweretsa YehovaNsanja ya Olonda—1989 | December 15
-
-
10. Mogwirizana ndi Ahebri 13:9, kodi mtima ukulimbikitsidwa ndi chiyani?
10 Chotero Ahebri anafunikira kupeŵa ‘kutengedwa ndi maphunzitso amitundumitundu ndi achilendo’ a Ayuda. (Agalatiya 5:1-6) Simwaziphunzitso zoterozo koma ‘mwa chisomo cha Mulungu ndi pamene mtima ungalimbitsidwe’ kotero kuti akhalebe okhazikika m’chowonadi. Mwachiwonekere ena anatsutsa ponena za zakudya ndi nsembe, popeza kuti Paulo ananena kuti mtima sunalimbitsidwe “ndi zakudya, zimene iwo adazitsata sanapindula nazo.” Mapindu auzimu amatuluka ku kudzipereka kwaumulungu ndi kuyamikira dipo, osati kuchokera ku kudera nkhaŵa kopambanitsa ponena za kudya zakudya zinazake ndi kusunga masiku ena. (Aroma 14:5-9) Ndiponso, nsembe ya Kristu inapangitsa nsembe za Alevi kusagwira ntchito.—Ahebri 9:9-14; 10:5-10.
-