-
Mafunso Ochokera kwa OŵerengaNsanja ya Olonda—2001 | October 1
-
-
Mtumwi Paulo anawalembera Akristu achihebri a zaka za zana loyamba kuti: “Utsalira mpumulo wa Sabata wa kwa anthu a Mulungu. Pakuti iye amene adaloŵa mpumulo wake, adapumulanso mwini wake ku ntchito zake, monganso Mulungu ku zake za Iye. Chifukwa chake tichite changu cha kuloŵa mpumulowo.”—Ahebri 4:9-11.
-
-
Mafunso Ochokera kwa OŵerengaNsanja ya Olonda—2001 | October 1
-
-
Tikabwerera ku zimene Paulo anawauza Ahebri, tikuona kuti ananena kuti “utsalira mpumulo wa Sabata wa kwa anthu a Mulungu,” ndipo analimbikitsa Akristu anzake kuti achite changu “cha kuloŵa mpumulowo.” Zimenezi zikusonyeza kuti nthaŵi imene Paulo analemba mawu ameneŵa, “tsiku lachisanu ndi chiŵiri” la kupumula kwa Mulungu, limene linayamba zaka pafupifupi 4,000 m’mbuyo mwakemo, linalipobe. Silidzatha mpaka cholinga cha Mulungu kwa anthu ndi dziko lapansi atachikwaniritsa bwinobwino pamapeto pa Ulamuliro wa Zaka 1,000 wa Yesu Kristu, yemwe ndi “mwini tsiku la Sabata.”—Mateyu 12:8; Chivumbulutso 20:1-6; 21:1-4.
-