Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Akulu—Chinjirizani Choikiziridwa Chanu
    Nsanja ya Olonda—1989 | September 15
    • 12. Kodi ndi uphungu wotani umene nthaŵi zina unafalitsidwa m’magazini ano womwe udzathandiza mkulu kupeŵa kugwiritsira ntchito lirime molakwa?

      12 Ndiponso, chinjirizani choikiziridwa chanu monga mkulu, mwa kupeŵa mbuna. Imodzi ya zimenezi ndiyo kugwiritsidwa ntchito kwa lilime molakwa monga mphunzitsi. Kufunika kwa kusamala pa mfundoyi kwagogomezeredwa kale ndi gulu la Yehova. Mwachitsanzo, m’kope lake la May 15, 1897, magazini ino inalongosola Yakobo 3:1-13 ndipo inati makamaka ponena za akulu: “Ngati iwo ali ndi lilime labwino iro lingakhale ngalande ya madalitso okulira, kukopera ziŵerengero zokulira kwa Ambuye, ku chowonadi ndi ku njira ya chilungamo; kapena, kumbali ina, ngati liri loipitsidwa ndi mphulupulu, lilime lingachite chifupifupi chivulazo chosaneneka​—chivulazo ku chikhulupiriro, ku makhalidwe, ku ntchito zabwino. Ziridi zowona, kuti aliyense wogwiritsira ntchito mphatso ya kuphunzitsa amadzinyamulira thayo lowonjezereka pamaso pa Mulungu ndi anthu. . . . Aliyense amene angakhale kasupe woyendamo Mawu a Mulungu, wonyamula dalitso ndi chitsitsimulo ndi nyonga, ayenera kutsimikizira kuti madzi oŵaŵa, ziphunzitso zonama zimene zingapangitse temberero, kuvulala​—kuchitira Mulungu mwano ndi kuipitsa Mawu ake​—sizipezanso mwa iwo ngalande yolankhulira. Posankha atsogoleri amisonkhano chiyeneretso cha ‘lilime,’ monga momwe chalembedwera panopa sichiyenera kunyalanyazidwa. A lilime lopyoza sayenera kusankhidwa, koma ofatsa, odekha amene, ‘amalamulira’ malilime awo ndi kuyesayesa kwambiri ‘kulankhula monga oimira Mulungu’ okha.” Nkofunika chotani nanga kuti mkulu agwiritsire ntchito lilime lake molondola!

  • Akulu—Chinjirizani Choikiziridwa Chanu
    Nsanja ya Olonda—1989 | September 15
    • 17, 18. Kodi ndiuphungu uti wofalitsidwa m’magazini ano zaka 80 zapitazo umene udakagwirabe ntchito kwa akulu Achikristu?

      17 Zoposa zaka 80 zapitazo, The Watchtower (March 1, 1909) inagwira mawu uphungu wapamwambapawo wa Paulo kwa akulu anzake ndi kuchitira ndemanga kuti: “Akulu kulikonse afunikira kulabadira mwapadera; chifukwa chakuti m’chiyeso chirichonse munthu woyanjidwa koposa ndi wotchuka koposa amakanthidwa ndi nkhonya ndi ziyeso zazikulu koposa. Chifukwa chake [Yakobo] akuchenjeza kuti, ‘Musakhale aphunzitsi ambiri a inu, abale, podziŵa kuti munthu akalandira kuyesedwa koipitsitsa.’ Ife, mofananamo, tikuchenjeza Akulu onse amene mu mtima ali oyera, opanda dyera, kuti asakhale ndi chinthu china chirichonse koma kokha chikondi ndi mafuno abwino kaamba ka anthu onse, ndi kuti adzazidwe mowonjezerekawonjezereka ndi zipatso ndi zisomo za Mzimu woyera, akumasamaliranso gulu. Kumbukirani, kuti gulu liri la Ambuye ndi kuti muli ndi thayo kwa Ambuye, ndi kwa ilo. Kumbukirani, kuti mufunikira kuyang’anira miyoyo yawo (ubwino wawo) monga awo ayenera kuŵerengera kwa Mbusa Wamkulu. Kumbukirani, kuti chinthu chachikulu koposa zonse ndicho Chikondi; ndipo pamene kuli kwakuti simukunyalanyaza ziphunzitso, labadirani mwapadera kugwira ntchito kwapadera kwa Mzimu wa Ambuye pakati pa ziŵalo zosiyanasiyana za Thupi lake, kuti mwakutero zikakhale ‘zokwanira kaamba ka choloŵa cha oyera m’kuwunika,’ ndipo, mogwirizana ndi chifuno cha Mulungu, musavutike ndi kukhumudwa m’tsiku iri loipa, koma, pokhala mutachita zonse, kuima okwanira mwa Kristu, Thupi lake, Ziŵalo zake, Ansembe Anzake, Oloŵa Nyumba Anzake.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena