-
Pitirizani Kuyenda m’Kuunika kwa UmulunguNsanja ya Olonda—1987
-
-
16. Kodi nchikondi chotani chimene sitiyenera kukhala nacho, koma nchiyani chimene chikakhala chowona ponena za ife ngati tinali ndi malingaliro ndi ziganizo za dziko?
16 Kaya ndife Akristu achicheperepo kapena achikulire, pali chikondi chimene sitiyenera kukhala nacho. (Werengani 1 Yohane 2:15-17) Sitiyenera ‘kukonda dziko kapena chirichonse mu iro.’ Mmalo mwake, tifunikira kupewa kukhala ochitidwa mawanga ndi chivundi cha anthu osalungama ndipo sitiyenera kupuma “mzimu” wake, kapena kusonkhezeredwa ndi mkhalidwe wake wofunga wauchimo. (Aefeso 2:1, 2; Yakobo 1:27) Ngati tinati tikhale ndi malingaliro ndi zikhumbo za dziko, “chikondi cha Atate” sichikanakhala mwa ife. (Yakobo 4:4) Imeneyo iridi mfundo yofunika mwapemphero, kodi sichoncho?
-
-
Pitirizani Kuyenda m’Kuunika kwa UmulunguNsanja ya Olonda—1987
-
-
19. Kodi nchiyani chimene chidzachitikira dziko lino, ndipo chenicheni chimenechi chiyenera kutiyambukira motani?
19 Kumbukirani kuti “dziko lapansi lipita” ndipo lidzawonongedwa. (2 Petro 3:6) Zilakolako zake ndi ziyembekezo zidzawonongeka limodzi nalo, monga momwe adzachitira olikonda. “Koma,” akutero Yohane, “iye amene achita chifuniro cha Mulungu akhala kunthawi yonse.” Chotero tiyeni tisunge chonulirapo cha moyo wamuyaya mwa ‘kukaniza zilakolako zadziko’ ndi kupitirizabe kuyenda m’kuunika kwa umulungu.—Tito 2:11-14.
-