-
Pitirizani Kuyenda m’Kuunika kwa UmulunguNsanja ya Olonda—1987
-
-
24. Kodi ndani amene ali “odzozedwa” ndi mzimu woyera, ndipo nchifukwa ninji iwo “safunikira aliyense kuwaphunzitsa”?
24 Kuyenda m’kuunika kwa umulungu ndi kusasochezedwa ndi ampatuko, tifunikira malangizo oyenerera auzimu. (Werengani 1 Yohane 2:26-29.) Obadwa ndi mzimuwo ali “odzozedwa” ndi mzimu woyera, afikiranso kudziwa Mulungu ndi Mwana wake, ndipo ‘sasowa kuti wina [wampatuko] awaphunzitse.’ Mwa kuwadzoza kwake ndi mzimu, Mulungu ‘akuphunzitsa’ Aisrayeli auzimu “za zinthu zonse” zofunika kumlambira movomerezeka. (Yohane 4:23, 24; 6:45) Tiri okondwera kuti monga Mboni za Yehova timalandira malangizo auzimu otero kuchokera kwa Mulungu kupyolera mwa “kapolo wokhulupirika ndi wanzeru.”—Mateyu 24:45-47.
-
-
Pitirizani Kuyenda m’Kuunika kwa UmulunguNsanja ya Olonda—1987
-
-
26 Popeza kuli kwakuti ife tsopano tiri mkati mwa “kukhala pafupi” kwa Yesu kodi tingatsimikizire motani kuti tiribe kanthu kakuchita nako manyazi ndipo tikuyendadi m’kuunika kwa Mulungu? Mwa ‘kugwiritsira ntchito chilungamo.’ ‘Ngati tidziwa kuti Mulungu ali wolungama,’ akutero Yohane, ‘tidziwa kuti aliyense wakuchita chilungamo wabadwa kuchokera kwa iye.’ ‘Kuchita chilungamo’ kumatanthauza kumvera malamulo a Mulungu, kupewa chisalungamo, ndi kukhala ndi phande m’ntchito zabwino kwambirizo monga kupanga ophunzira ndi kuthandiza okhulupirira anzathu. (Marko 13:10; Afilipi 4:14-19; 1 Timoteo 6:17, 18) “Kubadwa” ndi Mulungu kumatanthauza kukhala “wobadwanso” monga ana ake auzimu.—Yohane 3:3-8.
-