-
Muzinyansidwa ndi “Zinthu Zozama za Satana”Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
8. (a) Kodi Yesu anapereka uthenga wotani kwa “Yezebeli” wa ku Tiyatira? (b) Kodi azimayi ena achita zinthu zotani zosokoneza ena mumpingo masiku ano?
8 Yesu anapitiriza kuuza akulu a mpingo wa ku Tiyatira kuti: “Ndamupatsa nthawi kuti alape, koma sakufuna kulapa dama lake. Taona! Ndatsala pang’ono kumudwalitsa kwambiri, ndipo ochita naye chigololo ndiwaponya m’masautso aakulu, kupatulapo ngati atalapa ntchito zawo zofanana ndi za mayiyo.” (Chivumbulutso 2:21, 22) Mofanana ndi Yezebeli, amene zikuoneka kuti ankalamulira mwamuna wake Ahabu, ndipo kenako anachitira mwano Yehu, yemwe anatumidwa ndi Mulungu kuti adzamuphe, azimayi oipawa mwina ankanyengerera amuna awo komanso akulu kuti azichita zinthu zoipa. Zikuoneka kuti akulu mumpingo wa Tiyatira ankalekerera khalidwe losokoneza langati la Yezebeli limeneli. Yesu anawachenjeza mwamphamvu Akhristu amenewa, ndipo masiku ano chenjezoli likupitanso ku mpingo wa padziko lonse wa anthu a Yehova. Masiku ano, azimayi ena osafuna kuuzidwa zochita ofanana ndi Yezebeli, anyengererapo amuna awo kuti akhale ampatuko ndipo afika ngakhale potengera ku khoti atumiki a Yehova okhulupirika.—Yerekezerani ndi Yuda 5-8.
-
-
Muzinyansidwa ndi “Zinthu Zozama za Satana”Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
10. (a) N’chifukwa chiyani Yezebeli ndi ana ake anayenera kupatsidwa chilango? (b) Kodi ndi zinthu zoopsa ziti zimene zimachitikira anthu amene ndi ana a Yezebeli, ndipo anthu amenewo ayenera kuchita chiyani?
10 Popitiriza kufotokoza za “mayi uja Yezebeli,” Yesu anati: “Ana ake ndidzawapha ndi mliri wakupha, moti mipingo yonse idzadziwa kuti ineyo ndiye amene ndimafufuza impso ndi mitima, ndipo ndidzabwezera mmodzi ndi mmodzi wa inu malinga ndi ntchito zake.” (Chivumbulutso 2:23) Yesu anapatsa Yezebeli ndi ana ake nthawi yoti alape, koma iwo anapitirizabe khalidwe lawo lachiwerewere. Choncho anayenera kulangidwa. Pamenepa pali chenjezo lamphamvu kwa Akhristu masiku ano. Anthu amene amatsanzira Yezebeli, kaya ndi amuna kapena akazi, akudwala kwambiri mwauzimu. Iwo amakhala ana ake pophwanya mfundo za m’Baibulo zokhudza umutu ndi makhalidwe abwino, kapena posafuna kumva za ena n’kumanyalanyaza dongosolo limene gulu la Mulungu limachitira zinthu. Ngati munthu woteroyo ataitana akulu a mumpingo kuti amupempherere, “pemphero lachikhulupiriro lidzachiritsa wodwalayo, ndipo Yehova adzamulimbitsa.” Komabe iye ayenera kudzichepetsa n’kumachita zinthu zogwirizana ndi pempherolo. Ndipo aliyense asaganize kuti angapusitse Mulungu kapena Khristu poyesa kubisa khalidwe lachiwerewere kapena pochita utumiki mwakhama kwambiri kuti aphimbe tchimo.—Yakobo 5:14, 15.
11. Kodi mipingo masiku ano imathandizidwa bwanji kuti isalekerere akazi ofuna kusokoneza mumpingo?
11 N’zosangalatsa kuti mipingo yambiri ya Mboni za Yehova masiku ano imayesetsa kupewa khalidwe loipali. Akulu amakhala tcheru kwambiri kuti makhalidwe osagwirizana ndi dongosolo limene Mulungu amayendetsera zinthu komanso makhalidwe ena oipa, asalowerere mumpingo. Iwo amayesetsa kuthandiza abale ndi alongo amene ayamba kuchita zinthu zimene zingawavulaze mwauzimu, kuti asinthe mofulumira ndi kukhala olimba. (Agalatiya 5:16; 6:1) Oyang’anira achikhristu amenewa amachita zinthu molimba mtima ndiponso mwachikondi poletsa alongo amene ayamba kupanga timagulu tolimbikitsa ufulu wa amayi mumpingo. Komanso, malangizo a pa nthawi yake amaperekedwa nthawi ndi nthawi m’mabuku a Mboni za Yehova.a
12. Kodi Akhristu odzozedwa masiku ano amasonyeza bwanji mtima wosalekerera zoipa wofanana ndi wa Yehu?
12 Koma ngati munthu wachita chiwerewere, makamaka ngati wakhala akuchita zimenezi mobwerezabwereza, ayenera kuchotsedwa mumpingo akapanda kulapa. Tisaiwale kuti Yehu anali ndi mtima wosalekerera zoipa ndipo anachita khama kwambiri pofuna kuchotsa zinthu zonse zoipa zimene Yezebeli anayambitsa mu Isiraeli. Mofanana ndi Yehu, Akhristu odzozedwa masiku ano nawonso salekerera zoipa, ndipo amapereka chitsanzo chabwino kwa Akhristu a “nkhosa zina,” omwe ali ngati “Yehonadabu.” Pochita zimenezi, iwo amasonyeza kuti ndi osiyana kwambiri ndi atsogoleri a Matchalitchi Achikhristu, amene amangolekerera zoipa.—2 Mafumu 9:22, 30-37; 10:12-17.
-